Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Deuteronomo 18
  • Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

Zimene Zili Mʼbuku la Deuteronomo

      • Zimene ansembe ndi Alevi ankayenera kulandira (1-8)

      • Anawaletsa kuchita zamizimu (9-14)

      • Mneneri ngati Mose (15-19)

      • Mmene tingadziwire aneneri abodza (20-22)

Deuteronomo 18:1

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Nu 18:20, 24; De 10:9; Yos 13:14, 33; 1Ak 9:13

Deuteronomo 18:4

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Eks 23:19; Nu 18:8, 12; 2Mb 31:4; Ne 12:44

Deuteronomo 18:5

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Eks 28:1; Nu 3:10; De 10:8

Deuteronomo 18:6

Mawu a M'munsi

  • *

    Amenewa ndi malo amene Yehova wasankha kuti akhale malo olambirira.

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Nu 35:2
  • +De 12:5, 6; 16:2; Sl 26:8

Deuteronomo 18:7

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +2Mb 31:2

Deuteronomo 18:8

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Le 7:10

Deuteronomo 18:9

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Le 18:26; De 12:30

Deuteronomo 18:10

Mawu a M'munsi

  • *

    Mʼchilankhulo choyambirira, “wodutsitsa pamoto mwana wake wamwamuna kapena wamkazi.”

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +De 12:31; 2Mf 16:1, 3; 2Mb 28:1, 3; Sl 106:35-37; Yer 32:35
  • +2Mf 17:17; Mac 16:16
  • +Le 19:26; Mac 19:19
  • +Eze 21:21
  • +Eks 22:18

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Mungakhale Ndi Moyo Mpaka Kalekale, lesson 24

    Galamukani!,

    9/8/1993, tsa. 13

Deuteronomo 18:11

Mawu a M'munsi

  • *

    Mawu akuti ‘kuchesulaʼ amatanthauza kupweteka kapena kulepheretsa munthu kuchita chinachake mwa njira ya matsenga.

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Le 20:27; 1Mb 10:13
  • +Le 19:31
  • +1Sa 28:7-11; Yes 8:19; Aga 5:19, 20

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Kuyankha Mafunso a M’Baibulo, article 67

    Mungakhale Ndi Moyo Mpaka Kalekale, lesson 24

    Galamukani!,

    6/2012, ptsa. 10-11

Deuteronomo 18:12

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Mungakhale Ndi Moyo Mpaka Kalekale, lesson 24

Deuteronomo 18:13

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Mt 5:48; 2Pe 3:14

Deuteronomo 18:14

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Le 19:26; 2Mf 21:1, 2, 6
  • +Yos 13:22

Deuteronomo 18:15

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Ge 49:10; Nu 24:17; Lu 7:16; Yoh 1:45; 6:14; Mac 3:22; 7:37

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Kuyankha Mafunso a M’Baibulo,

    Nsanja ya Olonda,

    4/15/2009, ptsa. 24-28

    Galamukani!,

    4/8/2004, ptsa. 28-29

Deuteronomo 18:16

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Eks 19:17
  • +Eks 20:19

Deuteronomo 18:18

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Eks 34:28; Nu 12:3; Mt 4:1, 2; 11:29; Yoh 5:46
  • +Yoh 17:8
  • +Yoh 12:49; Ahe 1:2

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Kuyankha Mafunso a M’Baibulo,

    Nsanja ya Olonda,

    4/15/2009, ptsa. 24-28

    2/15/2000, ptsa. 22-24

    11/15/1991, ptsa. 28-31

Deuteronomo 18:19

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Mac 3:23

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Kuyankha Mafunso a M’Baibulo,

Deuteronomo 18:20

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +De 13:1-5; Yer 28:11-17

Mabaibulo Ena

Dinani pa nambala ya vesi kuti muone mavesi a m'Baibulo lina ofanana ndi vesilo.

Malemba Ena

Deut. 18:1Nu 18:20, 24; De 10:9; Yos 13:14, 33; 1Ak 9:13
Deut. 18:4Eks 23:19; Nu 18:8, 12; 2Mb 31:4; Ne 12:44
Deut. 18:5Eks 28:1; Nu 3:10; De 10:8
Deut. 18:6Nu 35:2
Deut. 18:6De 12:5, 6; 16:2; Sl 26:8
Deut. 18:72Mb 31:2
Deut. 18:8Le 7:10
Deut. 18:9Le 18:26; De 12:30
Deut. 18:10De 12:31; 2Mf 16:1, 3; 2Mb 28:1, 3; Sl 106:35-37; Yer 32:35
Deut. 18:102Mf 17:17; Mac 16:16
Deut. 18:10Le 19:26; Mac 19:19
Deut. 18:10Eze 21:21
Deut. 18:10Eks 22:18
Deut. 18:11Le 20:27; 1Mb 10:13
Deut. 18:11Le 19:31
Deut. 18:111Sa 28:7-11; Yes 8:19; Aga 5:19, 20
Deut. 18:13Mt 5:48; 2Pe 3:14
Deut. 18:14Le 19:26; 2Mf 21:1, 2, 6
Deut. 18:14Yos 13:22
Deut. 18:15Ge 49:10; Nu 24:17; Lu 7:16; Yoh 1:45; 6:14; Mac 3:22; 7:37
Deut. 18:16Eks 19:17
Deut. 18:16Eks 20:19
Deut. 18:18Eks 34:28; Nu 12:3; Mt 4:1, 2; 11:29; Yoh 5:46
Deut. 18:18Yoh 17:8
Deut. 18:18Yoh 12:49; Ahe 1:2
Deut. 18:19Mac 3:23
Deut. 18:20De 13:1-5; Yer 28:11-17
  • Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
  • Werengani mu Baibulo la Dziko Latsopano
  • 1
  • 2
  • 3
  • 4
  • 5
  • 6
  • 7
  • 8
  • 9
  • 10
  • 11
  • 12
  • 13
  • 14
  • 15
  • 16
  • 17
  • 18
  • 19
  • 20
  • 21
  • 22
Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
Deuteronomo 18:1-22

Deuteronomo

18 “Alevi omwe ndi ansembe, komanso fuko lonse la Levi, sadzapatsidwa gawo kapena cholowa pakati pa Aisiraeli. Iwo azidzadya nsembe zowotcha pamoto zoperekedwa kwa Yehova, zomwe ndi cholowa chake.+ 2 Choncho asamalandire cholowa pakati pa abale awo. Cholowa chawo ndi Yehova, mogwirizana ndi zimene anawauza.

3 Tsopano zinthu zimene ansembe azidzalandira kuchokera kwa anthu ndi izi: Amene akupereka nsembe ya ngʼombe kapena nkhosa, azipereka kwa wansembe mwendo wakutsogolo, nsagwada ndi chifu. 4 Aziperekanso kwa wansembe mbewu zawo zoyambirira kucha, vinyo wawo watsopano, mafuta awo ndi ubweya wa nkhosa zawo umene ameta moyambirira.+ 5 Yehova Mulungu wanu wamusankha pamodzi ndi ana ake, pakati pa mafuko anu onse, kuti atumikire mʼdzina la Yehova nthawi zonse.+

6 Koma Mlevi akatuluka mu umodzi mwa mizinda yanu mu Isiraeli kumene ankakhala,+ ndipo akufuna kupita kumalo amene Yehova wasankha,*+ 7 angathe kumatumikira kumeneko mʼdzina la Yehova Mulungu wake mofanana ndi Alevi onse, omwe ndi abale ake, amene akutumikira kumeneko pamaso pa Yehova.+ 8 Chakudya chimene azikalandira chikakhale chofanana ndi cha ansembe onse,+ kuwonjezera pa zimene walandira atagulitsa cholowa chimene analandira kwa makolo ake.

9 Mukakalowa mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani, musakaphunzire kuchita zinthu zonyansa zimene anthu a mitundu yakumeneko akuchita.+ 10 Pakati panu pasapezeke munthu wowotcha mwana wake pamoto,*+ wolosera,+ aliyense wochita zamatsenga,+ aliyense woombeza,+ wanyanga,+ 11 aliyense wochesula* ena, aliyense wofunsira kwa wolankhula ndi mizimu+ kapena wolosera zamʼtsogolo,+ kapena aliyense wofunsira kwa akufa.+ 12 Chifukwa aliyense wochita zimenezi ndi wonyansa kwa Yehova. Ndipo chifukwa chakuti anthu a mitundu ina akuchita zimenezi, Yehova Mulungu wanu akuwathamangitsa pamaso panu. 13 Mukhale opanda cholakwa pamaso pa Yehova Mulungu wanu.+

14 Mitundu imene mukuilanda dziko inkamvera anthu ochita zamatsenga+ ndi olosera.+ Koma Yehova Mulungu wanu sanakuloleni kuti muzichita zimenezi. 15 Yehova Mulungu wanu adzakupatsani mneneri ngati ine kuchokera pakati pa abale anu, ndipo mudzamumvere mneneri ameneyo.+ 16 Adzakupatsani mneneriyu poyankha zimene munapempha Yehova Mulungu wanu ku Horebe, tsiku limene munasonkhana kuphiri.+ Paja munapempha kuti, ‘Mutilole kuti tisamvenso mawu a Yehova Mulungu wathu kapena kuona moto waukuluwu, kuopera kuti tingafe.’+ 17 Ndiyeno Yehova anandiuza kuti, ‘Zimene anenazo ndi zabwino. 18 Ndidzawapatsa mneneri ngati iwe kuchokera pakati pa abale awo.+ Ndidzaika mawu anga mʼkamwa mwake,+ ndipo adzawauza zonse zimene ndidzamulamule.+ 19 Ndipo munthu amene sadzamvera mawu anga amene iye adzalankhule mʼdzina langa, adzayankha mlandu kwa ine.+

20 Ngati mneneri wina angadzikuze nʼkulankhula mʼdzina langa mawu amene sindinamulamule kuti alankhule, kapena kulankhula mʼdzina la milungu ina, mneneri ameneyo afe ndithu.+ 21 Koma munganene mumtima mwanu kuti: “Tidzadziwa bwanji kuti si Yehova amene walankhula mawuwo?” 22 Mneneri akalankhula mʼdzina la Yehova, koma zimene walankhulazo osachitika kapena kukwaniritsidwa, ndiye kuti si Yehova amene walankhula mawu amenewo. Mneneriyo walankhula mawu amenewo modzikuza ndipo musachite naye mantha.’”

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena