Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • 1 Mbiri 16:40
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 40 kuti azipereka nsembe zopsereza kwa Yehova nthawi zonse paguwa lansembe zopsereza, m’mawa ndi madzulo, malinga ndi zonse zolembedwa m’chilamulo cha Yehova chimene analamula Aisiraeli.+

  • 2 Mbiri 2:4
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 4 ine ndikumanga+ nyumba ya dzina+ la Yehova Mulungu wanga kuti ndiipatule+ ikhale yake. Ndikufuna kuti ndizifukiziramo mafuta onunkhira+ pamaso pake, ndi kuti nthawi zonse muzikhala mkate wosanjikiza.+ Ndiponso m’nyumbayo ndiziperekeramo nsembe zopsereza m’mawa ndi madzulo+ pa masabata,+ pa masiku okhala mwezi,+ ndi pa nyengo ya zikondwerero+ za Yehova Mulungu wathu. Zimenezi zizichitika mu Isiraeli mpaka kalekale.*+

  • 2 Mbiri 13:11
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 11 Iwo akufukiza nsembe zopsereza kwa Yehova m’mawa uliwonse ndi madzulo alionse.+ Akufukizanso mafuta onunkhira+ ndipo mikate yosanjikiza ili patebulo la golide woyenga bwino.+ Tilinso ndi choikapo nyale chagolide+ ndi nyale zake zimene amayatsa madzulo alionse.+ Tikuchita zimenezi chifukwa tikukwaniritsa udindo wathu+ kwa Yehova Mulungu wathu, koma inuyo mwamusiya.+

  • Danieli 9:27
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 27 “Mesiyayo* adzasungira anthu ambiri pangano+ kwa mlungu umodzi,+ kenako pakatikati pa mlunguwo adzathetsa nsembe zanyama ndi nsembe zina zoperekedwa ngati mphatso.+

      “Wowonongayo+ adzabwera pamapiko a zinthu zonyansa, ndipo zimene Mulungu wagamula zidzakhuthulidwanso pa chowonongedwacho+ kufikira chitafafanizidwa.”

  • Aheberi 7:27
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 27 Iye safunikira kupereka tsiku ndi tsiku+ nsembe za machimo ake choyamba,+ kenako za anthu ena, monga mmene amachitira akulu a ansembe.+ (Iye anachita zimenezi kamodzi+ kokha pamene anadzipereka yekha nsembe.+ Nsembe imene anapereka motereyi ithandiza anthu mpaka muyaya.)

  • Aheberi 10:11
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 11 Komanso, wansembe aliyense amaima pamalo ake+ kuti achite ntchito yotumikira ena ndi kupereka nsembe zimodzimodzizo mobwerezabwereza,+ popeza zimenezi sizingachotseretu machimo.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena