Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Ekisodo 30:34
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 34 Ndiyeno Yehova anapitiriza kulankhula ndi Mose kuti: “Tenga zonunkhira izi:+ madontho a sitakate,* onika, mafuta onunkhira a galibanamu ndi lubani*+ weniweni. Zonsezi zikhale za muyezo wofanana.

  • 2 Mbiri 13:11
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 11 Iwo akufukiza nsembe zopsereza kwa Yehova m’mawa uliwonse ndi madzulo alionse.+ Akufukizanso mafuta onunkhira+ ndipo mikate yosanjikiza ili patebulo la golide woyenga bwino.+ Tilinso ndi choikapo nyale chagolide+ ndi nyale zake zimene amayatsa madzulo alionse.+ Tikuchita zimenezi chifukwa tikukwaniritsa udindo wathu+ kwa Yehova Mulungu wathu, koma inuyo mwamusiya.+

  • Chivumbulutso 8:4
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 4 Pamenepo, utsi wa zofukizazo unakwera pamaso pa Mulungu kuchokera m’dzanja la mngeloyo limodzi ndi mapemphero+ a oyera.

  • Levitiko 16:13
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 13 Akatero, aziika zofukizazo pamoto umene uli pamaso pa Yehova,+ ndipo utsi wa zofukizazo uzikuta chivundikiro cha Likasa,+ chimene chili pa Umboni,+ kuopera kuti angafe.

  • Numeri 16:40
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 40 Eleazara anachita izi kuti timalatato tikhale chikumbutso kwa ana a Isiraeli, kuti munthu aliyense amene si mbadwa+ ya Aroni asayandikire kwa Yehova+ kukafukiza nsembe. Anateronso kuti pasapezeke wina aliyense wochita zimene Kora limodzi ndi gulu lake+ anachita. Eleazara anachita zonse monga mmene Yehova anamuuzira kudzera kwa Mose.

  • 1 Samueli 2:28
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 28 Kholo lakolo ndinalisankha kuchokera m’mafuko onse a Isiraeli kuti akhale wansembe wanga,+ ndipo azikwera paguwa langa lansembe+ kuti utsi wa nsembezo uzikwera kumwamba, kutinso azivala efodi pamaso panga. Ndinachita izi kuti ndipatse nyumba ya kholo lako nsembe zonse zotentha ndi moto za ana a Isiraeli.+

  • 1 Mbiri 23:13
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 13 Ana aamuna a Amuramu anali Aroni+ ndi Mose.+ Koma Aroni anapatulidwa+ kuti iye ndi ana ake aziyeretsa Malo Oyera Koposa,+ mpaka kalekale. Komanso kuti azifukiza nsembe+ yautsi pamaso pa Yehova, kumutumikira,+ ndi kupereka madalitso+ m’dzina lake mpaka kalekale.

  • Luka 1:9
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 9 malinga ndi mwambo wa ansembe, inali nthawi yake yakuti azilowa m’nyumba yopatulika ya Yehova,+ n’kupereka nsembe zofukiza.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena