Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Ekisodo 15:3
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    •  3 Yehova ndi wankhondo.+ Dzina lake ndi Yehova.+

  • 1 Samueli 17:45
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 45 Poyankha Davide anauza Mfilisitiyo kuti: “Iwe ukubwera kwa ine ndi lupanga, mkondo ndi nthungo,+ koma ine ndikubwera kwa iwe m’dzina la Yehova wa makamu,+ Mulungu wa asilikali a Isiraeli, amene iweyo wam’tonza.+

  • Salimo 96:8
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    •  8 M’patseni Yehova ulemerero woyenera dzina lake.+

      Tengani mphatso ndi kulowa m’mabwalo ake.+

  • Salimo 135:13
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 13 Inu Yehova, dzina lanu lidzakhalapo mpaka kalekale.+

      Inu Yehova, dzina lanu* lidzakhalapo ku mibadwomibadwo.+

  • Hoseya 12:5
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 5 Iye ndi Yehova Mulungu wa makamu.+ Yehova ndilo dzina lake lomukumbukira nalo.+

  • Mateyu 21:9
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 9 Koma khamu la anthu, limene linali patsogolo pake ndi m’mbuyo mwake linali kufuula kuti: “M’pulumutseni+ Mwana wa Davide!+ Wodalitsidwa iye wobwera m’dzina la Yehova!*+ M’pulumutseni kumwambamwambako!”+

  • Yohane 17:26
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 26 Ine ndachititsa kuti iwo adziwe dzina lanu+ ndipo ndidzapitiriza kuwadziwitsa dzinalo kuti chikondi chimene munandikonda nacho chikhale mwa iwo, inenso ndikhale wogwirizana ndi iwo.”+

  • Aroma 10:13
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 13 Pakuti “aliyense amene adzaitana pa dzina la Yehova* adzapulumuka.”+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena