Salimo 18:6 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 6 Pa nthawi ya zowawa zanga ndinaitana Yehova,Ndinafuulira Mulungu wanga kuti andithandize.+Iye anamva mawu anga ali m’kachisi wake.+Pamenepo makutu ake anamva kulira kwanga kopempha thandizo.+ Salimo 27:1 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 27 Yehova ndiye kuwala+ kwanga ndi chipulumutso changa.+Ndingaopenso ndani?+Yehova ndiye malo a chitetezo cha moyo wanga.+Ndingachitenso mantha ndi ndani?+ Salimo 31:1 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 31 Ndathawira kwa inu Yehova.+Musalole kuti ndichite manyazi.+Ndipulumutseni chifukwa cha chilungamo chanu.+ Salimo 31:9 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 9 Ndikomereni mtima inu Yehova, pakuti ndasautsika kwambiri.+Diso langa lafooka chifukwa cha chisoni,+ chimodzimodzinso moyo wanga ndi m’mimba mwanga.+ Salimo 34:19 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 19 Masoka a munthu wolungama ndi ochuluka,+Koma Yehova amamupulumutsa ku masoka onsewo.+ Salimo 43:5 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 5 N’chifukwa chiyani ukutaya mtima, moyo wangawe?+Ndipo n’chifukwa chiyani ukusautsika mkati mwanga?Yembekezera Mulungu,+Ndipo ndidzamutamanda pakuti iye ndiye mpulumutsi wanga wamkulu ndi Mulungu wanga.+ Salimo 56:4 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 4 Popeza kuti ndine wogwirizana ndi Mulungu, ndidzatamanda mawu ake.+Ine ndimadalira Mulungu, sindidzaopa.+Kodi munthu angandichite chiyani?+ Salimo 143:5 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 5 Ndakumbukira masiku akale.+Ndasinkhasinkha zochita zanu zonse,+Ndipo ndakhala ndikuganizira ntchito ya manja anu ndi mtima wonse.+ Miyambo 18:10 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 10 Dzina la Yehova ndi nsanja yolimba.+ Wolungama amathawira mmenemo ndipo amatetezedwa.+ Habakuku 3:18 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 18 Ine ndidzakondwerabe mwa Yehova+ ndipo ndidzasangalala mwa Mulungu wachipulumutso changa.+ Luka 22:43 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 43 Pamenepo mngelo wochokera kumwamba anaonekera kwa iye ndi kumulimbikitsa.+
6 Pa nthawi ya zowawa zanga ndinaitana Yehova,Ndinafuulira Mulungu wanga kuti andithandize.+Iye anamva mawu anga ali m’kachisi wake.+Pamenepo makutu ake anamva kulira kwanga kopempha thandizo.+
27 Yehova ndiye kuwala+ kwanga ndi chipulumutso changa.+Ndingaopenso ndani?+Yehova ndiye malo a chitetezo cha moyo wanga.+Ndingachitenso mantha ndi ndani?+
31 Ndathawira kwa inu Yehova.+Musalole kuti ndichite manyazi.+Ndipulumutseni chifukwa cha chilungamo chanu.+
9 Ndikomereni mtima inu Yehova, pakuti ndasautsika kwambiri.+Diso langa lafooka chifukwa cha chisoni,+ chimodzimodzinso moyo wanga ndi m’mimba mwanga.+
5 N’chifukwa chiyani ukutaya mtima, moyo wangawe?+Ndipo n’chifukwa chiyani ukusautsika mkati mwanga?Yembekezera Mulungu,+Ndipo ndidzamutamanda pakuti iye ndiye mpulumutsi wanga wamkulu ndi Mulungu wanga.+
4 Popeza kuti ndine wogwirizana ndi Mulungu, ndidzatamanda mawu ake.+Ine ndimadalira Mulungu, sindidzaopa.+Kodi munthu angandichite chiyani?+
5 Ndakumbukira masiku akale.+Ndasinkhasinkha zochita zanu zonse,+Ndipo ndakhala ndikuganizira ntchito ya manja anu ndi mtima wonse.+