-
Yesaya 37:24Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
24 Kudzera mwa antchito ako watonza Yehova ndipo wanena kuti,+
Ndi magaleta anga ankhondo ambiri, ine,+
Ineyo ndidzakwera ndithu madera amapiri mpaka pamwamba.+
Ndidzafika kumadera akutali kwambiri a Lebanoni+
Ndipo ndidzadula mitengo yake ya mkungudza italiitali, ndi mitengo yake yabwino kwambiri yofanana ndi mkungudza.+
Ndidzalowa kumalo ake okhala akutali kwambiri, kunkhalango yokongola.+
-
-
Ezekieli 31:8Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
8 Mitengo ina ya mkungudza sinafanane ndi mtengo umenewu m’munda wa Mulungu.+ Nthambi zikuluzikulu za mitengo ina yooneka ngati mkungudza, sizinafanane ndi za mtengo umenewu. Nthambi za mitengo ya katungulume sizinafanane ndi nthambi za mtengo umenewu. Panalibenso mtengo wina m’munda wa Mulungu umene unali wokongola ngati mtengo umenewu.+
-