Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Yesaya 14:8
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 8 Ngakhale mitengo ya mlombwa+ yakondwa poona zimene zakuchitikira. Nayonso mitengo ya mkungudza ya ku Lebanoni yakondwa, ndipo yonseyi yanena kuti, ‘Kuyambira pamene unagona pansi, palibenso munthu wodula mitengo+ amene wabwera kudzatidula.’

  • Yesaya 37:24
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 24 Kudzera mwa antchito ako watonza Yehova ndipo wanena kuti,+

      Ndi magaleta anga ankhondo ambiri, ine,+

      Ineyo ndidzakwera ndithu madera amapiri mpaka pamwamba.+

      Ndidzafika kumadera akutali kwambiri a Lebanoni+

      Ndipo ndidzadula mitengo yake ya mkungudza italiitali, ndi mitengo yake yabwino kwambiri yofanana ndi mkungudza.+

      Ndidzalowa kumalo ake okhala akutali kwambiri, kunkhalango yokongola.+

  • Yesaya 60:13
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 13 “Ulemerero wa Lebanoni udzabwera kwa iwe. Mtengo wofanana ndi mkungudza, mtengo wa ashi, ndiponso mtengo wa paini zidzabwera pa nthawi imodzi,+ kuti zikongoletse malo anga opatulika,+ ndipo ine ndidzalemekeza malo oikapo mapazi anga.+

  • Ezekieli 31:8
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 8 Mitengo ina ya mkungudza sinafanane ndi mtengo umenewu m’munda wa Mulungu.+ Nthambi zikuluzikulu za mitengo ina yooneka ngati mkungudza, sizinafanane ndi za mtengo umenewu. Nthambi za mitengo ya katungulume sizinafanane ndi nthambi za mtengo umenewu. Panalibenso mtengo wina m’munda wa Mulungu umene unali wokongola ngati mtengo umenewu.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena