Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Deuteronomo 6:12
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 12 samala kuti usaiwale+ Yehova amene anakutulutsa m’dziko la Iguputo, m’nyumba yaukapolo.

  • Yobu 31:24
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 24 Ngati ndayesa golide chinthu chodalira,

      Kapena ngati ndanena kwa golide kuti, ‘Ndimadalira iwe,’+

  • Salimo 52:7
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    •  7 Munthu wamphamvu wotere sadalira Mulungu monga malo ake achitetezo,+

      Koma amadalira kuchuluka kwa chuma chake,+

      Ndipo chitetezo chake amachipeza m’mavuto amene iyeyo amawachititsa.+

  • Miyambo 11:4
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 4 Zinthu zamtengo wapatali zidzakhala zopanda phindu pa tsiku la mkwiyo woopsa,+ koma chilungamo n’chimene chidzapulumutse munthu ku imfa.+

  • Miyambo 11:28
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 28 Wodalira chuma chake adzagwa,+ koma anthu olungama adzasangalala ngati masamba a zomera.+

  • Miyambo 23:5
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 5 Kodi maso ako amayang’anitsitsa chuma, pomwe icho sichichedwa kuchoka?+ Chifukwa ndithu chimadzipangira mapiko ngati a chiwombankhanga n’kuulukira kumwamba.+

  • Mateyu 6:19
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 19 “Lekani kudziunjikira chuma+ padziko lapansi, pamene njenjete* ndi dzimbiri zimawononga, ndiponso pamene mbala zimathyola ndi kuba.

  • Mateyu 6:24
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 24 “Kapolo sangatumikire ambuye awiri, pakuti adzadana ndi mmodzi ndi kukonda winayo,+ kapena adzakhulupirika kwa mmodzi ndi kunyoza winayo. Simungathe kutumikira Mulungu ndi Chuma nthawi imodzi.+

  • Maliko 8:36
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 36 Kunena zoona, pali phindu lanji ngati munthu atapeza zinthu zonse za m’dzikoli koma n’kutaya moyo wake?+

  • Luka 12:15
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 15 Kenako anauza anthuwo kuti: “Khalani maso ndipo chenjerani ndi kusirira kwa nsanje kwamtundu uliwonse,+ chifukwa ngakhale munthu atakhala ndi zochuluka chotani, moyo wake suchokera m’zinthu zimene ali nazo.”+

  • 1 Timoteyo 6:17
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 17 Lamula achuma+ a m’nthawi* ino kuti asakhale odzikweza,+ ndiponso kuti asamadalire chuma chosadalirika,+ koma adalire Mulungu, amene amatipatsa mowolowa manja zinthu zonse kuti tisangalale.+

  • 1 Yohane 2:16
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 16 Pakuti chilichonse cha m’dziko,+ monga chilakolako cha thupi,+ chilakolako cha maso+ ndi kudzionetsera ndi zimene munthu ali nazo pa moyo wake,+ sizichokera kwa Atate, koma kudziko.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena