Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Deuteronomo 32:4
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    •  4 Iye ndi Thanthwe, ndipo ntchito yake ndi yangwiro,+

      Njira zake zonse ndi zolungama.+

      Mulungu wokhulupirika,+ amene sachita chosalungama.+

      Iye ndi wolungama ndi wowongoka.+

  • Salimo 5:4
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    •  4 Pakuti inu sindinu Mulungu wokondwera ndi zoipa,+

      Palibe munthu woipa amene angakhale ndi inu ngakhale kwa kanthawi kochepa.+

  • Salimo 71:19
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 19 Chilungamo chanu, inu Mulungu chafika kumwamba.+

      Tikanena za zinthu zazikulu zimene munachita,+

      Inu Mulungu, ndani angafanane ndi inu?+

  • Salimo 97:2
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    •  2 Mitambo ndi mdima wandiweyani zamuzungulira.+

      Chilungamo ndi chiweruzo ndizo malo okhazikika a mpando wake wachifumu.+

  • Salimo 145:17
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 17 Yehova ndi wolungama m’njira zake zonse,+

      Ndipo ndi wokhulupirika m’ntchito zake zonse.+

  • Miyambo 16:12
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 12 Kuchita zinthu zoipa kumanyansa mafumu,+ chifukwa mpando wachifumu umakhazikika ndi chilungamo.+

  • Chivumbulutso 15:3
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 3 Iwo akuimba nyimbo ya Mose+ kapolo wa Mulungu, ndi nyimbo ya Mwanawankhosa,+ yakuti:

      “Ntchito zanu n’zazikulu ndi zodabwitsa,+ inu Yehova Mulungu Wamphamvuyonse.+ Njira zanu ndi zolungama ndi zoona,+ inu Mfumu yamuyaya.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena