Ekisodo 32:4 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 4 Pamenepo iye analandira golideyo kuchokera kwa anthuwo ndipo pogwiritsa ntchito chosemera, anam’panga+ kukhala fano la mwana wa ng’ombe+ lopangidwa ndi golide wosungunula. Zitatero iwo anayamba kunena kuti: “Uyu ndiye Mulungu wanu, Aisiraeli inu, amene anakutulutsani m’dziko la Iguputo.”+ Salimo 97:7 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 7 Onse amene akupembedza chifaniziro chilichonse achite manyazi.+Amene amadzitama chifukwa cha milungu yopanda pake achite manyazi.+Muweramireni, inu milungu yonse.+ Yesaya 1:29 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 29 Pakuti anthu adzachita manyazi ndi mitengo ikuluikulu imene inu munali kuilakalaka,+ ndipo mudzagwetsa nkhope zanu chifukwa cha minda imene mwasankha.+ Yesaya 44:11 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 11 Anzake onse adzachita manyazi,+ ndipotu amisiriwo ndi anthu ochokera kufumbi. Onsewo adzasonkhana pamodzi.+ Adzaima chilili. Adzachita mantha. Onsewo adzachitira limodzi manyazi.+ Yesaya 44:17 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 17 Koma mtengo wotsalawo wapangira mulungu, wapangira chifaniziro chake chosema. Wachiweramira ndi kuchigwadira n’kumapemphera pamaso pake kuti: “Ndipulumutseni, pakuti ndinu mulungu wanga.”+ Yesaya 45:16 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 16 Anthu adzachita manyazi ndipo onsewo adzanyozeka. Anthu opanga mafano adzayenda monyozeka onse pamodzi.+ Yeremiya 2:26 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 26 “Monga mmene mbala imachitira manyazi ikagwidwa, anthu a m’nyumba ya Isiraeli nawonso achita manyazi,+ iwowo, mafumu awo, akalonga awo, ansembe awo ndiponso aneneri awo.+
4 Pamenepo iye analandira golideyo kuchokera kwa anthuwo ndipo pogwiritsa ntchito chosemera, anam’panga+ kukhala fano la mwana wa ng’ombe+ lopangidwa ndi golide wosungunula. Zitatero iwo anayamba kunena kuti: “Uyu ndiye Mulungu wanu, Aisiraeli inu, amene anakutulutsani m’dziko la Iguputo.”+
7 Onse amene akupembedza chifaniziro chilichonse achite manyazi.+Amene amadzitama chifukwa cha milungu yopanda pake achite manyazi.+Muweramireni, inu milungu yonse.+
29 Pakuti anthu adzachita manyazi ndi mitengo ikuluikulu imene inu munali kuilakalaka,+ ndipo mudzagwetsa nkhope zanu chifukwa cha minda imene mwasankha.+
11 Anzake onse adzachita manyazi,+ ndipotu amisiriwo ndi anthu ochokera kufumbi. Onsewo adzasonkhana pamodzi.+ Adzaima chilili. Adzachita mantha. Onsewo adzachitira limodzi manyazi.+
17 Koma mtengo wotsalawo wapangira mulungu, wapangira chifaniziro chake chosema. Wachiweramira ndi kuchigwadira n’kumapemphera pamaso pake kuti: “Ndipulumutseni, pakuti ndinu mulungu wanga.”+
16 Anthu adzachita manyazi ndipo onsewo adzanyozeka. Anthu opanga mafano adzayenda monyozeka onse pamodzi.+
26 “Monga mmene mbala imachitira manyazi ikagwidwa, anthu a m’nyumba ya Isiraeli nawonso achita manyazi,+ iwowo, mafumu awo, akalonga awo, ansembe awo ndiponso aneneri awo.+