Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Yesaya 23:1
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 23 Uthenga wokhudza Turo:+ Lirani mofuula inu zombo za ku Tarisi,+ chifukwa chakuti mzindawo wasakazidwa ndipo sulinso doko. Sulinso malo oti mungafikepo.+ Anthu amva zimenezi ali kudziko la Kitimu.+

  • Yeremiya 25:22
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 22 mafumu onse a Turo,+ mafumu onse a Sidoni+ ndi mafumu a pachilumba cha m’nyanja.

  • Ezekieli 26:2
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 2 “Iwe mwana wa munthu, Turo+ wanena Yerusalemu+ kuti, ‘Eyaa! Zakhala bwino! Mzindawo wathyoledwa.+ Mzinda umene unali kukopa anthu a mitundu ina+ wathyoledwa. Tsopano ine zinthu zindiyendera bwino. Ndilemera chifukwa mzindawo wawonongedwa.’+

  • Yoweli 3:4
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 4 “Tsopano ndili nawenso chiyani iwe Turo ndi Sidoni+ ndiponso inu nonse okhala m’chigawo cha Filisitiya?+ Kodi zimenezi ndi zimene mukundipatsa monga mphoto yanga? Ngati mukundipatsa zimenezi, ine ndidzakubwezerani mwamsanga ndiponso mofulumira zimene mwandichitirazo.+

  • Amosi 1:9
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 9 “Yehova wanena kuti, ‘Popeza kuti Turo+ anapanduka mobwerezabwereza, sindidzamusinthira chigamulo changa. Sindidzamusinthira chigamulocho chifukwa chakuti anapereka ku Edomu gulu lonse la anthu ogwidwa ukapolo, ndiponso chifukwa chakuti sanakumbukire pangano la pa ubale.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena