Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • 1 Mafumu 9:8
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 8 Nyumba iyi idzakhala bwinja.+ Aliyense wodutsa pafupi nayo adzayang’ana modabwa+ ndi kuimba mluzu n’kunena kuti, ‘N’chifukwa chiyani Yehova anachita zimenezi padzikoli ndi panyumbayi?’+

  • 2 Mafumu 25:9
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 9 Iye anatentha nyumba ya Yehova,+ nyumba ya mfumu,+ nyumba zonse za mu Yerusalemu,+ ndi nyumba ya munthu aliyense wotchuka.+

  • 2 Mbiri 7:21
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 21 Ndipo nyumba iyi ikadzakhala bwinja,+ aliyense wodutsa pafupi nayo adzayang’ana modabwa,+ ndipo ndithu adzati, ‘N’chifukwa chiyani Yehova anachita zimenezi padzikoli ndi panyumbayi?’+

  • 2 Mbiri 36:19
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 19 Iyo inatentha nyumba ya Mulungu woona+ ndi kugwetsa mpanda+ wa Yerusalemu. Ababulowo anatenthanso ndi moto nyumba zonse zokhala ndi mipanda yolimba kwambiri za mzindawo ndi zinthu zake zonse zabwinozabwino,+ mpaka zonse zinawonongedwa.+

  • Salimo 74:8
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    •  8 Iwo, ngakhalenso ana awo, onse pamodzi anena mumtima mwawo kuti:

      “Malo onse olambiriramo a Mulungu ayenera kutenthedwa m’dzikoli.”+

  • Salimo 79:1
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 79 Inu Mulungu, anthu a mitundu ina alowa m’dziko limene ndilo cholowa chanu.+

      Aipitsa kachisi wanu woyera.+

      Awononga Yerusalemu ndi kumusandutsa bwinja.+

  • Yeremiya 26:18
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 18 “Mika+ wa ku Moreseti+ nayenso anali kunenera m’masiku a Hezekiya mfumu ya Yuda.+ Iye anauza anthu onse a mu Yuda kuti, ‘Yehova wa makamu wanena kuti: “Ziyoni adzagawulidwa ngati munda,+ ndipo Yerusalemu adzangokhala milu ya mabwinja.+ Phiri la nyumba ya Mulungu lidzakhala ngati zitunda za m’nkhalango.”’+

  • Maliro 2:7
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    •  7 Yehova wataya guwa lake lansembe.+ Iye wanyoza malo ake opatulika.+

      Wapereka m’manja mwa adani makoma* a nsanja zake zokhalamo.+

      Iwo afuula m’nyumba ya Yehova ngati pa tsiku lachikondwerero.+

  • Ezekieli 24:21
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 21 ‘Uza nyumba ya Isiraeli kuti: “Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa, wanena kuti, ‘Ine ndidetsa malo anga opatulika,+ chinthu chimene mumachinyadira kwambiri,+ chinthu chosiririka kwa inu,+ ndiponso chinthu chimene mumachichitira chifundo. Ana anu aamuna ndi aakazi amene munawasiya m’mbuyo adzaphedwa ndi lupanga.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena