Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • 1 Mafumu 9:8
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 8 Nyumba iyi idzakhala bwinja.+ Aliyense wodutsa pafupi nayo adzayang’ana modabwa+ ndi kuimba mluzu n’kunena kuti, ‘N’chifukwa chiyani Yehova anachita zimenezi padzikoli ndi panyumbayi?’+

  • 2 Mbiri 36:19
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 19 Iyo inatentha nyumba ya Mulungu woona+ ndi kugwetsa mpanda+ wa Yerusalemu. Ababulowo anatenthanso ndi moto nyumba zonse zokhala ndi mipanda yolimba kwambiri za mzindawo ndi zinthu zake zonse zabwinozabwino,+ mpaka zonse zinawonongedwa.+

  • Salimo 74:3
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    •  3 Pitani kumalo amene awonongedwa.+

      M’malo oyera, mdani wachitira zoipa china chilichonse.+

  • Salimo 79:1
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 79 Inu Mulungu, anthu a mitundu ina alowa m’dziko limene ndilo cholowa chanu.+

      Aipitsa kachisi wanu woyera.+

      Awononga Yerusalemu ndi kumusandutsa bwinja.+

  • Yesaya 64:11
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 11 Nyumba yathu yoyera ndiponso yokongola+ imene makolo athu anali kukutamandiranimo,+ yasanduka chinthu chofunika kuchitentha pamoto,+ ndipo zinthu zathu zonse zabwinozabwino+ zasakazidwa.

  • Yeremiya 7:14
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 14 ndidzachita zofanana ndi zimene ndinachita ku Silo.+ Ndidzachita zimenezi panyumba imene ikutchedwa ndi dzina langa,+ imene inu mukuidalira,+ ndiponso malo amene ndinapatsa inu ndi makolo anu.

  • Maliro 1:10
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 10 Mdani watambasula dzanja lake n’kutenga zinthu+ zake zonse zabwino.

      Yerusalemu waona mitundu ina itabwera ndi kulowa m’malo ake opatulika,+

      Mitundu imene munalamula kuti isalowe mumpingo wanu.

  • Maliro 2:7
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    •  7 Yehova wataya guwa lake lansembe.+ Iye wanyoza malo ake opatulika.+

      Wapereka m’manja mwa adani makoma* a nsanja zake zokhalamo.+

      Iwo afuula m’nyumba ya Yehova ngati pa tsiku lachikondwerero.+

  • Mika 3:12
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 12 Chotero Ziyoni adzagawulidwa ngati munda chifukwa cha anthu inu ndipo Yerusalemu adzangokhala milu ya mabwinja.+ Phiri la nyumba ya Mulungu lidzakhala ngati zitunda za m’nkhalango.

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena