Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • 2 Mbiri 36:18
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 18 Mfumuyo inatenga ziwiya zonse,+ zazikulu+ ndi zazing’ono, za m’nyumba ya Mulungu woona. Inatenganso chuma+ cha m’nyumba ya Yehova, chuma cha mfumu+ ndi cha akalonga ake. Inatenga chilichonse n’kupita nacho ku Babulo.

  • Yesaya 39:6
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 6 ‘Kukubwera masiku amene zinthu zonse zimene zili m’nyumba mwako, ndi zonse zimene makolo ako akhala akusunga kufikira lero, anthu adzazitenga n’kupita nazo ku Babulo.+ Palibe chidzatsale,’+ watero Yehova.

  • Yeremiya 15:13
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 13 Ndidzapereka chuma chanu anthu inu ndi zinthu zanu zamtengo wapatali kwa wofunkha+ popanda malipiro. Ndidzatero chifukwa cha machimo anu onse amene munachita m’dziko lanu lonse.+

  • Yeremiya 20:5
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 5 Ndipo ndidzatenga zinthu zonse zosungidwa mumzindawu, katundu wawo yense, zinthu zonse zamtengo wapatali ndi chuma chonse cha mafumu a Yuda, n’kuzipereka m’manja mwa adani awo.+ Ndipo adaniwo adzafunkha zinthu zimenezi ndi kupita nazo ku Babulo.+

  • Yeremiya 52:17
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 17 Zipilala zamkuwa+ zimene zinali panyumba ya Yehova, zotengera zokhala ndi mawilo+ ndi chosungiramo madzi chamkuwa+ zimene zinali m’nyumba ya Yehova, Akasidi anaziphwanyaphwanya n’kutenga mkuwa wakewo kupita nawo ku Babulo.+

  • Yeremiya 52:19
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 19 Mkulu wa asilikali olondera mfumu uja anatenga mabeseni,+ zopalira moto, mbale zolowa,+ ndowa zochotsera phulusa, zoikapo nyale,+ zikho ndi mbale zinanso zolowa zomwe zinali zagolide weniweni,+ komanso zomwe zinali zasiliva weniweni.+

  • Danieli 1:2
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 2 Kenako Yehova anapereka Yehoyakimu mfumu ya Yuda m’manja mwake.+ Anaperekanso kwa iye zina mwa ziwiya+ za m’nyumba ya Mulungu woona moti Nebukadinezara anazitengera kudziko la Sinara,+ kunyumba ya mulungu wake. Ziwiya zimenezi anakaziika m’nyumba ya mulungu wake yosungiramo chuma.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena