Yeremiya 5:31 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 31 Aneneri akulosera monama,+ ndipo ansembe akupondereza anthu ndi mphamvu zawo.+ Anthu anga nawonso akukonda zimenezi.+ Ndipo kodi anthu inu mudzachita chiyani pamapeto pake?”+ Yeremiya 27:9 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 9 “‘“‘Anthu inu musamvere aneneri,+ ochita zamaula, olota maloto,+ ochita zamatsenga ndi obwebweta+ amene ali pakati panu ndipo akukuuzani kuti: “Anthu inu simudzatumikira mfumu ya Babulo.”+ Maliro 2:14 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 14 Aneneri ako aona masomphenya achabechabe ndi opanda pake+ onena za iwe.Iwo sanaulule zolakwa zako kuti akuteteze n’cholinga choti usatengedwe kupita ku ukapolo,+Koma anali kuona masomphenya achabechabe ndi osocheretsa+ onena za iwe. Maliro 4:13 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 13 Zimenezi zinachitika chifukwa cha machimo a aneneri ake ndi zolakwa za ansembe ake,+Amene anakhetsa magazi a anthu olungama a mumzindawo.+ Ezekieli 22:28 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 28 Aneneri a mumzindawo apaka laimu machimo a atsogoleriwo.+ Aona masomphenya onama+ ndipo akuloserera atsogoleriwo zinthu zabodza.+ Iwo akunena kuti: “Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa, wanena kuti,” pamene Yehova sananene chilichonse.
31 Aneneri akulosera monama,+ ndipo ansembe akupondereza anthu ndi mphamvu zawo.+ Anthu anga nawonso akukonda zimenezi.+ Ndipo kodi anthu inu mudzachita chiyani pamapeto pake?”+
9 “‘“‘Anthu inu musamvere aneneri,+ ochita zamaula, olota maloto,+ ochita zamatsenga ndi obwebweta+ amene ali pakati panu ndipo akukuuzani kuti: “Anthu inu simudzatumikira mfumu ya Babulo.”+
14 Aneneri ako aona masomphenya achabechabe ndi opanda pake+ onena za iwe.Iwo sanaulule zolakwa zako kuti akuteteze n’cholinga choti usatengedwe kupita ku ukapolo,+Koma anali kuona masomphenya achabechabe ndi osocheretsa+ onena za iwe.
13 Zimenezi zinachitika chifukwa cha machimo a aneneri ake ndi zolakwa za ansembe ake,+Amene anakhetsa magazi a anthu olungama a mumzindawo.+
28 Aneneri a mumzindawo apaka laimu machimo a atsogoleriwo.+ Aona masomphenya onama+ ndipo akuloserera atsogoleriwo zinthu zabodza.+ Iwo akunena kuti: “Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa, wanena kuti,” pamene Yehova sananene chilichonse.