Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Yeremiya 5:31
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 31 Aneneri akulosera monama,+ ndipo ansembe akupondereza anthu ndi mphamvu zawo.+ Anthu anga nawonso akukonda zimenezi.+ Ndipo kodi anthu inu mudzachita chiyani pamapeto pake?”+

  • Yeremiya 6:13
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 13 “Pakuti aliyense wa iwo, kuyambira wamng’ono mpaka wamkulu akupeza phindu lachinyengo.+ Kuyambira mneneri mpaka wansembe, aliyense wa iwo akuchita zachinyengo.+

  • Yeremiya 14:14
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 14 Ndiyeno Yehova anandiyankha kuti: “Aneneriwo akulosera monama m’dzina langa.+ Ine sindinawatume, kuwalamula, kapena kulankhula nawo.+ Maulosi amene akukuuzaniwo anthu inu, ndiwo masomphenya onama, maula, mawu opanda pake+ ndi chinyengo cha mumtima mwawo.+

  • Yeremiya 23:11
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 11 “Aneneri ndi ansembe, onse aipitsidwa+ ndipo m’nyumba mwanga ndapezamo zoipa zimene akuchita,”+ watero Yehova.

  • Maliro 2:14
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 14 Aneneri ako aona masomphenya achabechabe ndi opanda pake+ onena za iwe.

      Iwo sanaulule zolakwa zako kuti akuteteze n’cholinga choti usatengedwe kupita ku ukapolo,+

      Koma anali kuona masomphenya achabechabe ndi osocheretsa+ onena za iwe.

  • Mika 3:11
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 11 Atsogoleri a mumzindawo saweruza asanalandire chiphuphu+ ndipo ansembe ake amaphunzitsa kuti apeze malipiro.+ Aneneri ake amalosera kuti apeze ndalama.+ Komatu iwo amadalira Yehova ndipo amanena kuti: “Kodi Yehova sali pakati pathu?+ Choncho tsoka silidzatigwera.”+

  • Zefaniya 3:4
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 4 Aneneri ake anali amwano ndi achinyengo.+ Ansembe ake anaipitsa zinthu zopatulika ndipo anaphwanya chilamulo.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena