-
Yesaya 31:1Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
31 Tsoka kwa anthu amene akupita ku Iguputo kukapempha thandizo.+ Iwo akudalira mahatchi wamba+ ndi kukhulupirira magaleta ankhondo,+ chifukwa chakuti ndi ambiri. Akudaliranso mahatchi akuluakulu chifukwa chakuti ndi amphamvu kwambiri, koma sanayang’ane kwa Woyera wa Isiraeli ndipo sanafunefune Yehova.+
-
-
Yeremiya 44:12Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
12 Ine ndigwira otsala a Yuda amene anatsimikiza mtima kulowa m’dziko la Iguputo ndi kukhala mmenemo monga alendo,+ moti onse adzathera m’dziko la Iguputo.+ Iwo adzakanthidwa ndi lupanga ndipo onsewo, osasiyapo aliyense, adzatha chifukwa cha njala yaikulu.+ Adzafa ndi lupanga komanso njala yaikulu. Iwo adzakhala otembereredwa, chinthu chodabwitsa ndi chotonzedwa.+
-