Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Yeremiya 49:8
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 8 Thawani!+ Bwererani! Pitani kumalo otsika kuti mukakhale kumeneko,+ inu okhala ku Dedani!+ Pakuti Esau ndidzamugwetsera tsoka pa nthawi yomulanga.+

  • Maliro 4:22
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 22 Iwe mwana wamkazi wa Ziyoni, chilango chimene anakupatsa chifukwa cha zolakwa zako chatha.+ Sadzakutenganso kupita nawe ku ukapolo.+

      Tsopano iwe mwana wamkazi wa Edomu, Mulungu watembenukira kwa iwe kuti aone zolakwa zako. Machimo ako wawaika poyera.+

  • Ezekieli 36:5
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 5 Mawu amene Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa, wanena ndi akuti, ‘Ndithudi, ndidzadzudzula anthu otsala a mitundu ina ndiponso Edomu yense nditakwiya kwambiri.+ Ndidzadzudzula amene anatenga dziko langa kuti likhale lawo. Iwo analitenga akusangalala+ komanso kunyoza mumtima mwawo+ poona kuti atenga dzikolo ndi malo ake odyetserako ziweto.’”’+

  • Amosi 1:11
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 11 “Yehova wanena kuti, ‘Chifukwa chakuti Edomu wandipandukira mobwerezabwereza,+ sindidzamusinthira chigamulo changa. Sindidzamusinthira chigamulocho chifukwa chakuti anathamangitsa m’bale wake ndi lupanga,+ sanasonyeze chifundo,+ akupitiriza kukhadzulakhadzula zinthu ali wokwiya komanso akukhalabe wokwiya mosalekeza.+

  • Obadiya 1
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 1 Tsopano awa ndiwo masomphenya a Obadiya:

      Zimene Yehova Ambuye Wamkulu Koposa wanena zokhudza Edomu ndi izi:+ “Ife tamva uthenga wochokera kwa Yehova ndipo nthumwi yatumidwa kwa anthu a mitundu ina kukanena kuti: ‘Nyamukani anthu inu, tiyeni timuukire ndi kumenyana naye.’”+

  • Obadiya 10
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 10 Chifukwa chakuti m’bale wako Yakobo unam’chitira zachiwawa,+ manyazi adzakugwira.+ Iwe udzawonongedwa ndipo sudzakhalaponso mpaka kalekale.*+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena