Mateyu
3 M’masiku amenewo, Yohane M’batizi+ anapita m’chipululu+ cha Yudeya n’kuyamba kulalikira. 2 Iye anali kulalikira kuti: “Lapani,+ pakuti ufumu wakumwamba wayandikira.”+ 3 Mneneri Yesaya ananenera za iyeyu+ m’mawu awa: “Tamverani! Winawake akufuula m’chipululu kuti, ‘Konzani+ njira ya Yehova anthu inu! Wongolani misewu yake.’” 4 Koma Yohane ameneyu, anali kuvala chovala chaubweya wa ngamila+ ndi lamba wachikopa+ m’chiuno mwake. Chakudya chake chinali dzombe+ ndi uchi.+ 5 Choncho anthu ochokera ku Yerusalemu ndi ku Yudeya konse ndiponso ochokera m’midzi yonse yapafupi ndi Yorodano anali kubwera kwa iye. 6 Iye anali kuwabatiza mumtsinje wa Yorodano,+ ndipo anthuwo anali kuulula machimo awo poyera.
7 Pamene Yohane anaona Afarisi ndi Asaduki+ ambiri akubwera ku ubatizowo, anawauza kuti: “Ana a njoka inu,+ ndani wakuchenjezani kuti muthawe mkwiyo umene ukubwerawo?+ 8 Ndiyetu mubale zipatso zosonyeza kulapa.+ 9 Musamadzinyenge kuti, ‘Tili ndi atate wathu Abulahamu.’+ Pakuti ndikukuuzani kuti Mulungu angathe kuutsira Abulahamu+ ana kuchokera kumiyala iyi. 10 Nkhwangwa+ yaikidwa kale pamizu yamitengo. Chotero mtengo uliwonse wosabala zipatso zabwino udulidwa+ ndi kuponyedwa pamoto.+ 11 Inetu ndikukubatizani m’madzi+ chifukwa cha kulapa kwanu,+ koma amene akubwera+ m’mbuyo mwanga ndi wamphamvu kuposa ine, ndipo sindili woyenera kumuvula nsapato zake.+ Ameneyo adzakubatizani ndi mzimu woyera+ komanso ndi moto.+ 12 Fosholo yake youluzira mankhusu* ili m’manja mwake, ndipo malo ake opunthirapo mbewu adzawayeretseratu kuti mbee! Tirigu adzamututira m’nkhokwe,+ koma mankhusu adzawatentha+ ndi moto umene sungazimitsidwe.”
13 Kenako Yesu anabwera kwa Yohane ku Yorodano kuchokera ku Galileya,+ kuti iye amubatize.+ 14 Koma Yohane anayesa kumuletsa ponena kuti: “Ine ndiye wofunika kubatizidwa ndi inu, nanga inu mukubweranso kwa ine kodi?” 15 Poyankha Yesu anamuuza kuti: “Pa nthawi ino lola kuti zikhale choncho, chifukwa n’koyenera kwa ife kutero kuti tikwaniritse chilungamo chonse.”+ Atatero, anasiya kumuletsa. 16 Atabatizidwa, nthawi yomweyo Yesu anavuuka m’madzimo. Pamenepo kumwamba kunatseguka,+ ndipo Yohane anaona mzimu wa Mulungu ukutsika ngati nkhunda+ kudzamutera.+ 17 Panamvekanso mawu+ ochokera kumwamba onena kuti: “Uyu ndiye Mwana wanga+ wokondedwa,+ amene ndimakondwera naye.”+