Ekisodo 22:25 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 25 “Ukabwereketsa ndalama kwa anthu anga, kwa munthu wovutika amene ali pafupi ndi iwe,+ usakhale ngati munthu wopereka ngongole yakatapira* kwa iye. Usafunepo chiwongoladzanja.+ Deuteronomo 23:19 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 19 “M’bale wako usamulipiritse chiwongoladzanja+ pa ndalama, chakudya+ kapena chilichonse chimene munthu angafunepo chiwongoladzanja. Nehemiya 5:7 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 7 Choncho ndinayamba kuganiza mumtima mwanga ndipo ndinapeza kuti anthu olemekezeka ndi atsogoleri anali olakwa.+ Pamenepo ndinawauza kuti: “Nonsenu mukuumiriza abale anu kukupatsani chiwongoladzanja chokwera kwambiri.”+ Kenako ndinaitanitsa msonkhano waukulu chifukwa cha iwowa.+ Salimo 15:5 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 5 Sapereka ndalama zake kuti alandire chiwongoladzanja,+Ndipo salandira chiphuphu kuti akhotetse mlandu wa munthu wosalakwa.+Wochita zinthu zimenezi, sadzagwedezeka konse.+ Miyambo 28:8 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 8 Munthu amene amachulukitsa zinthu zamtengo wapatali kuchokera ku chiwongoladzanja ndi katapira,*+ amangosungira zinthuzo munthu amene amakomera mtima anthu onyozeka.+ Ezekieli 18:13 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 13 Iye amakongoza zinthu zake mwa katapira+ ndipo amalandira chiwongoladzanja.+ Ndithudi iye sadzakhala ndi moyo chifukwa wachita zinthu zonyansa zonsezi.+ Adzaphedwa ndithu, ndipo magazi ake adzakhala pamutu pake.+
25 “Ukabwereketsa ndalama kwa anthu anga, kwa munthu wovutika amene ali pafupi ndi iwe,+ usakhale ngati munthu wopereka ngongole yakatapira* kwa iye. Usafunepo chiwongoladzanja.+
19 “M’bale wako usamulipiritse chiwongoladzanja+ pa ndalama, chakudya+ kapena chilichonse chimene munthu angafunepo chiwongoladzanja.
7 Choncho ndinayamba kuganiza mumtima mwanga ndipo ndinapeza kuti anthu olemekezeka ndi atsogoleri anali olakwa.+ Pamenepo ndinawauza kuti: “Nonsenu mukuumiriza abale anu kukupatsani chiwongoladzanja chokwera kwambiri.”+ Kenako ndinaitanitsa msonkhano waukulu chifukwa cha iwowa.+
5 Sapereka ndalama zake kuti alandire chiwongoladzanja,+Ndipo salandira chiphuphu kuti akhotetse mlandu wa munthu wosalakwa.+Wochita zinthu zimenezi, sadzagwedezeka konse.+
8 Munthu amene amachulukitsa zinthu zamtengo wapatali kuchokera ku chiwongoladzanja ndi katapira,*+ amangosungira zinthuzo munthu amene amakomera mtima anthu onyozeka.+
13 Iye amakongoza zinthu zake mwa katapira+ ndipo amalandira chiwongoladzanja.+ Ndithudi iye sadzakhala ndi moyo chifukwa wachita zinthu zonyansa zonsezi.+ Adzaphedwa ndithu, ndipo magazi ake adzakhala pamutu pake.+