Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Oweruza 3:10
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 10 Mzimu+ wa Yehova unakhala pa iye, ndipo anakhala woweruza wa Isiraeli. Atapita kunkhondo, Yehova anapereka Kusani-risataimu mfumu ya Siriya m’manja mwake, moti anam’gonjetsa.+

  • Oweruza 11:29
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 29 Tsopano mzimu wa Yehova unabwera pa Yefita+ ndipo anadutsa m’dera la Giliyadi, m’dera la Manase, ndi m’dera la Mizipe wa ku Giliyadi.+ Atadutsa m’dera la Mizipe wa ku Giliyadi anafika kwa ana a Amoni.

  • Oweruza 13:25
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 25 Kenako mzimu wa Yehova+ unayamba kugwira ntchito pa iye ku Mahane-dani+ pakati pa Zora+ ndi Esitaoli.+

  • Oweruza 14:6
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 6 Ndiyeno mzimu wa Yehova unayamba kugwira ntchito pa iye,+ moti anakhadzula mkangowo pakati ngati mmene munthu angakhadzulire kamwana ka mbuzi. Iye analibe chida chilichonse m’manja mwake. Zimene anachitazi sanauze bambo kapena mayi ake.

  • Oweruza 15:14
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 14 Choncho iye anafika ku Lehi, ndipo Afilisiti atamuona anafuula mokondwera.+ Pamenepo, mzimu wa Yehova+ unayamba kugwira ntchito pa iye, ndipo zingwe zimene anam’manga nazo manja zija zinaduka ngati ulusi wowauka ndi moto,+ moti zinadukaduka ndi kugwa.

  • Yesaya 63:11
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 11 Iwo anayamba kukumbukira masiku akale, masiku a Mose mtumiki wake, ndipo anafunsa kuti: “Kodi amene anawatulutsa m’nyanja+ pamodzi ndi abusa a anthu ake uja, ali kuti?+ Ali kuti amene anaika mzimu wake woyera mwa iye?+

  • Zekariya 4:6
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 6 Choncho iye anandiuza kuti: “Yehova wauza Zerubabele kuti, ‘“Kuti zinthu zonsezi zichitike, sipakufunika gulu lankhondo,+ kapena mphamvu,+ koma mzimu wanga,”+ watero Yehova wa makamu.

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena