Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Genesis 33:11
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 11 Chonde, landirani mphatso yokufunirani mafuno abwinoyi kuchokera kwa ine,+ chifukwa Mulungu wandikomera mtima, ndipo wandipatsa chilichonse.”+ Anamuumirizabe mpaka analandira mphatsoyo.+

  • 1 Samueli 25:18
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 18 Nthawi yomweyo, Abigayeli+ anafulumira kutenga mitanda 200 ya mkate, mitsuko iwiri ikuluikulu ya vinyo,+ anapha nkhosa zisanu,+ anatenganso miyezo ya seya* isanu ya tirigu wokazinga,+ mphesa zouma zoumba pamodzi 100+ ndi nkhuyu zouma zoumba pamodzi 200+ ndi kuzikweza pa abulu.

  • 1 Samueli 30:26
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 26 Davide atafika ku Zikilaga anatumiza zina mwa zofunkhazo kwa mabwenzi ake,+ akulu a ku Yuda, n’kunena kuti: “Landirani mphatso*+ iyi kuchokera pa zimene tafunkha kwa adani a Yehova.”

  • 2 Mafumu 5:15
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 15 Kenako iye pamodzi ndi gulu lake lonse anabwerera kwa munthu wa Mulungu woona+ uja. Anaima pamaso pake n’kunena kuti: “Tsopano ndadziwa ndithu kuti, padziko lonse lapansi kulibenso kwina kumene kuli Mulungu kupatula ku Isiraeli kokha.+ Ndiye landirani mphatso+ kuchokera kwa ine mtumiki wanu.”

  • Miyambo 18:16
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 16 Mphatso ya munthu imam’tsegulira khomo lalikulu,+ ndipo imakam’fikitsa ngakhale pamaso pa anthu olemekezeka.+

  • Miyambo 25:21
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 21 Ngati munthu wodana nawe ali ndi njala, um’patse chakudya. Ngati ali ndi ludzu, um’patse madzi akumwa,+

  • Miyambo 25:22
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 22 pakuti ukumuunjikira makala amoto pamutu pake,+ ndipo Yehova adzakupatsa mphoto.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena