Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • 2 Mafumu 25:15
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 15 Mkulu wa asilikali olondera mfumu uja anatenga zopalira moto ndi mbale zolowa zomwe zinali zagolide weniweni,+ komanso zomwe zinali zasiliva weniweni.+

  • 2 Mbiri 36:18
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 18 Mfumuyo inatenga ziwiya zonse,+ zazikulu+ ndi zazing’ono, za m’nyumba ya Mulungu woona. Inatenganso chuma+ cha m’nyumba ya Yehova, chuma cha mfumu+ ndi cha akalonga ake. Inatenga chilichonse n’kupita nacho ku Babulo.

  • Ezara 1:7
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 7 Komanso, Mfumu Koresi inabweretsa ziwiya za nyumba ya Yehova.+ Ziwiyazo n’zimene Nebukadinezara anatenga ku Yerusalemu+ n’kukaziika m’kachisi wa mulungu wake.+

  • Yeremiya 27:16
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 16 Ndiyeno ndinalankhula ndi ansembe ndi anthu ena onsewa kuti: “Yehova wanena kuti, ‘Musamvere mawu a aneneri anu amene akulosera kwa inu kuti: “Taonani! Ziwiya za m’nyumba ya Yehova zibwezedwa kuchokera ku Babulo posachedwapa!”+ Pakuti iwo akulosera kwa inu monama.+

  • Yeremiya 52:19
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 19 Mkulu wa asilikali olondera mfumu uja anatenga mabeseni,+ zopalira moto, mbale zolowa,+ ndowa zochotsera phulusa, zoikapo nyale,+ zikho ndi mbale zinanso zolowa zomwe zinali zagolide weniweni,+ komanso zomwe zinali zasiliva weniweni.+

  • Danieli 1:2
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 2 Kenako Yehova anapereka Yehoyakimu mfumu ya Yuda m’manja mwake.+ Anaperekanso kwa iye zina mwa ziwiya+ za m’nyumba ya Mulungu woona moti Nebukadinezara anazitengera kudziko la Sinara,+ kunyumba ya mulungu wake. Ziwiya zimenezi anakaziika m’nyumba ya mulungu wake yosungiramo chuma.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena