38 zofukizira za amuna amene anafa+ chifukwa cha kuchimwa. Azisule kuti zikhale timalata topyapyala n’kukutira nato guwa lansembe,+ popeza anafika nazo pamaso pa Yehova, ndipo zakhala zopatulika. Timalatato tikhale chikumbutso kwa ana a Isiraeli.’”+
20 Moyo umene ukuchimwawo ndi umene udzafe.+ Mwana sadzakhala ndi mlandu uliwonse pa zolakwa za bambo ake. Bambo sadzakhala ndi mlandu uliwonse pa zolakwa za mwana wake.+ Chilungamo cha munthu wolungama chidzakhala pa iye,+ ndipo zoipa za munthu woipa zidzakhala pamutu pa woipayo.+