Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Yobu 31:24
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 24 Ngati ndayesa golide chinthu chodalira,

      Kapena ngati ndanena kwa golide kuti, ‘Ndimadalira iwe,’+

  • Salimo 17:14
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 14 Ndipulumutseni kwa anthu ndi dzanja lanu, inu Yehova,+

      Ndipulumutseni kwa anthu a m’nthawi* ino,+ amene gawo lawo lili m’moyo uno.+

      Anthu amene mimba zawo mwazidzaza ndi chuma chanu chobisika,+

      Amene ali ndi ana aamuna ochuluka,+

      Ndipo amakundikira ana awo chuma.+

  • Salimo 52:7
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    •  7 Munthu wamphamvu wotere sadalira Mulungu monga malo ake achitetezo,+

      Koma amadalira kuchuluka kwa chuma chake,+

      Ndipo chitetezo chake amachipeza m’mavuto amene iyeyo amawachititsa.+

  • Salimo 62:10
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 10 Musadalire chizolowezi chobera ena mwachinyengo,+

      Ndipo musakhale wachabechabe chifukwa chochita uchifwamba.+

      Ngati chuma chanu chachuluka, mtima wanu wonse usakhale pachumacho.+

  • Yeremiya 9:23
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 23 Yehova wanena kuti: “Munthu wanzeru asadzitamande chifukwa cha nzeru zake.+ Munthu wamphamvu asadzitamande chifukwa cha mphamvu zake.+ Munthu wachuma asadzitamande chifukwa cha chuma chake.”+

  • 1 Timoteyo 6:17
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 17 Lamula achuma+ a m’nthawi* ino kuti asakhale odzikweza,+ ndiponso kuti asamadalire chuma chosadalirika,+ koma adalire Mulungu, amene amatipatsa mowolowa manja zinthu zonse kuti tisangalale.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena