Numeri
34 Yehova analankhulanso ndi Mose, kuti: 2 “Lamula ana a Isiraeli, uwauze kuti, ‘Pamene mukukalowa m’dziko la Kanani,+ nawa malire a dziko+ limene mudzalandire ngati cholowa chanu.+
3 “‘Chigawo chanu chakum’mwera chiyenera kuyambira kuchipululu cha Zini, kumalire a Edomu.+ Malire anu a kum’mwera ayenera kuchokera kumathero a Nyanja Yamchere,+ kum’mawa. 4 Malirewo akadutse kum’mwera kwa chitunda cha Akirabimu+ kulowera ku Zini, n’kuloweranso kum’mwera kwa Kadesi-barinea.+ Kenako akakhotere ku Hazara-adara+ n’kukafika ku Azimoni. 5 Ndiyeno malirewo akalowere kuchigwa* cha Iguputo+ mpaka kukafika ku Nyanja Yaikulu.+
6 “‘Malire anu a kumadzulo+ akatsatire gombe la Nyanja Yaikulu.
7 “‘Malire anu a kumpoto akayende motere: Mukalembe malirewo kuchokera ku Nyanja Yaikulu mpaka kuphiri la Hora.+ 8 Kuchokera kuphiri la Hora, mukalembe malirewo akafike ku Hamati,+ mpaka ku Zedadi.+ 9 Malirewo akafike ku Zifironi, mpaka ku Hazara-enani.+ Awa ndiwo adzakhale malire anu a kumpoto.
10 “‘Ndiyeno mukalembe malire anu a kum’mawa kuyambira ku Hazara-enani mpaka ku Sefamu. 11 Malirewo akatsike kuchokera ku Sefamu kulowera ku Ribila, kum’mawa kwa Aini. Akatsikebe mpaka akagunde malo otsetsereka a kum’mawa kwa nyanja ya Kinereti.*+ 12 Malirewo akatsike ndithu mpaka kumtsinje wa Yorodano, ndipo akathere ku Nyanja Yamchere.+ Limeneli ndilo dziko lanu+ ndi malire ake olizungulira.’”
13 Chotero Mose anauza ana a Isiraeli kuti: “Ili ndilo dziko limene ligawidwe kwa inu mwa maere+ monga cholowa chanu. Lidzagawidwa kwa inu monga momwe Yehova analamulira kuti lipatsidwe kwa mafuko 9 ndi hafu.+ 14 Fuko la ana a Rubeni mwa mabanja a makolo awo, ndi fuko la ana a Gadi mwa mabanja a makolo awo, alandira kale cholowa chawo. Ndiponso hafu ya fuko la Manase, nawonso alandira kale cholowa chawo.+ 15 Mafuko awiri ndi hafuwo alandira kale cholowa chawo kudera la kum’mawa kwa Yorodano, moyang’anana ndi Yeriko.”+
16 Yehova anapitiriza kulankhula ndi Mose, kuti: 17 “Amuna amene akakugawireni malo monga cholowa chanu, mayina awo ndi awa: Wansembe Eleazara+ ndi Yoswa mwana wa Nuni.+ 18 Musankhe mtsogoleri mmodzi pa fuko lililonse, kuti akathandize kugawa cholowa cha malo.+ 19 Amunawo mayina awo ndi awa: Pa fuko la Yuda,+ Kalebe mwana wa Yefune, + 20 pa fuko la ana a Simiyoni,+ Semuyeli mwana wa Amihudi, 21 pa fuko la Benjamini,+ Elidadi mwana wa Kisiloni, 22 pa fuko la ana a Dani,+ mtsogoleri Buki mwana wa Yogili, 23 pa ana a Yosefe+ ku fuko la ana a Manase,+ mtsogoleri Hanieli mwana wa Efodi, 24 pa fuko la ana a Efuraimu,+ mtsogoleri Kemueli mwana wa Sipitana, 25 pa fuko la ana a Zebuloni,+ mtsogoleri Elizafana mwana wa Paranaki, 26 pa fuko la ana a Isakara,+ mtsogoleri Palitiyeli mwana wa Azani, 27 pa fuko la ana a Aseri,+ mtsogoleri Ahihudi mwana wa Selomi, 28 ndipo pa fuko la ana a Nafitali,+ mtsogoleri Pedaheli mwana wa Amihudi.” 29 Amenewa ndiwo amuna amene Yehova analamula kuti akagawire malo ana a Isiraeli, kuti akakhale ndi malo awoawo m’dziko la Kanani.+