Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • 2 Mafumu 14:9
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 9 Yehoasi mfumu ya Isiraeli itamva inamuyankha Amaziya mfumu ya Yuda kuti: “Chitsamba chaminga cha ku Lebanoni chinatumiza uthenga kwa mtengo wa mkungudza+ wa ku Lebanoni, wakuti, ‘Ndipatse mwana wako wamkazi kuti mwana wanga wamwamuna amukwatire.’ Koma nyama yakuthengo ya ku Lebanoni inadutsa pamenepo n’kupondaponda chitsamba chaminga chija.+

  • Yesaya 2:13
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 13 Lidzafikira mikungudza yonse ya ku Lebanoni+ yodzikweza ndi yokwezeka. Lidzafikiranso mitengo yonse ikuluikulu ya ku Basana.+

  • Yesaya 37:24
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 24 Kudzera mwa antchito ako watonza Yehova ndipo wanena kuti,+

      Ndi magaleta anga ankhondo ambiri, ine,+

      Ineyo ndidzakwera ndithu madera amapiri mpaka pamwamba.+

      Ndidzafika kumadera akutali kwambiri a Lebanoni+

      Ndipo ndidzadula mitengo yake ya mkungudza italiitali, ndi mitengo yake yabwino kwambiri yofanana ndi mkungudza.+

      Ndidzalowa kumalo ake okhala akutali kwambiri, kunkhalango yokongola.+

  • Ezekieli 31:3
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 3 Wafanana ndi Msuri. Wafanana ndi mtengo wa mkungudza wa ku Lebanoni,+ wanthambi zikuluzikulu zokongola,+ wanthambi za masamba ambiri zopereka mthunzi, mtengo wautali kwambiri+ umene nsonga yake inafika m’mitambo.+

  • Amosi 2:9
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 9 “‘Koma ine ndinawononga Aamori+ chifukwa cha anthu anga. Aamoriwo misinkhu yawo inali yofanana ndi mitengo ya mkungudza ndipo mphamvu zawo zinali zofanana ndi za mitengo ikuluikulu.+ Ndinawononga zipatso zawo m’mwamba ndiponso mizu yawo pansi.+

  • Zekariya 11:2
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 2 Lira mofuula, iwe mtengo wofanana ndi mkungudza, chifukwa chakuti mtengo wa mkungudza wagwa, ndiponso mitengo ikuluikulu yawonongedwa.+ Lirani mofuula, inu mitengo ikuluikulu ya ku Basana, chifukwa nkhalango yowirira kwambiri ija yawonongedwa.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena