Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Genesis 9:6
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 6 Aliyense wokhetsa magazi a munthu, nayenso magazi ake adzakhetsedwa ndi munthu,+ chifukwa Mulungu anapanga munthu m’chifaniziro chake.

  • Oweruza 9:5
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 5 Atatero anapita kunyumba ya bambo ake ku Ofira+ ndi kupha abale ake,+ ana aamuna 70 a Yerubaala, pamwala umodzi. Koma sanaphe Yotamu, mwana wamng’ono kwambiri mwa ana aamuna a Yerubaala, chifukwa anali atabisala.

  • Oweruza 9:24
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 24 Mulungu analola zimenezi kuti chiwawa chimene anachitira ana aamuna 70 a Yerubaala chiwabwerere pamutu pawo,+ ndi kuti aike magazi a anawo pa Abimeleki m’bale wawo chifukwa ndiye anawapha.+ Analolanso zimenezi kuti chiwawacho chibwerere pamutu pa nzika za Sekemu, chifukwa zinalimbikitsa+ Abimeleki kuti aphe abale ake.

  • 1 Samueli 25:39
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 39 Ndiyeno Davide anamva kuti Nabala wamwalira. Atatero, iye anati: “Adalitsike Yehova amene wandiweruzira mlandu+ ndi kundimasula ku chitonzo+ cha Nabala, komanso wagwira ine mtumiki wake kuti ndisachite choipa.+ Yehova wabwezera zoipa za Nabala pamutu pake!”+ Pamenepo Davide anatumiza anthu kuti akamufunsirire Abigayeli, kuti akhale mkazi wake.+

  • Salimo 58:10
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 10 Wolungama adzasangalala chifukwa chakuti waona oipa akupatsidwa chilango.+

      Adzasambitsa mapazi ake m’magazi a anthu oipa.+

  • Salimo 94:23
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 23 Iye adzawabwezera zoipa zawo,+

      Ndipo adzawakhalitsa chete mwa kuwadzetsera masoka okonza okha.+

      Yehova Mulungu wathu adzawakhalitsa chete.+

  • Miyambo 5:22
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 22 Woipa adzagwidwa ndi zolakwa zake zomwe,+ ndipo adzamangidwa m’zingwe za tchimo lake lomwe.+

  • Agalatiya 6:7
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 7 Musanyengedwe,+ Mulungu sapusitsika.+ Chilichonse chimene munthu wafesa, adzakololanso chomwecho.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena