1 Samueli 11:15 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 15 Choncho anthu onse anapita ku Giligala ndipo analonga Sauli kukhala mfumu pamaso pa Yehova ku Giligalako. Kenako anapereka nsembe zachiyanjano pamaso pa Yehova+ kumeneko, ndipo Sauli pamodzi ndi amuna onse a Isiraeli anali osangalala kwambiri.+ 1 Samueli 13:13 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 13 Pamenepo Samueli anauza Sauli kuti: “Wachita chinthu chopusa.+ Sunatsatire lamulo+ limene Yehova Mulungu wako anakupatsa.+ Ukanatsatira lamulo limeneli, Yehova akanalimbitsa ufumu wako pa Isiraeli mpaka kalekale. 1 Samueli 15:26 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 26 Samueli anamuyankha kuti: “Sindibwerera nawe chifukwa wakana mawu a Yehova, ndipo Yehova wakukana kuti upitirize kukhala mfumu ya Isiraeli.”+ 1 Samueli 16:23 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 23 Ndiyeno mzimu woipa wa Mulungu ukafika pa Sauli, Davide anali kutenga zeze ndi kumuimbira. Akatero, Sauli anali kupeza bwino, ndipo mzimu woipawo unali kum’chokera.+ 1 Samueli 28:7 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 7 Pamapeto pake, Sauli anauza atumiki ake kuti: “Ndifufuzireni mkazi waluso polankhula ndi mizimu,+ ndipo ine ndipita kukalankhula naye.” Pamenepo atumiki ake anamuuza kuti: “Ku Eni-dori alipo mkazi waluso polankhula ndi mizimu.”+ 1 Samueli 31:4 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 4 Kenako Sauli anauza womunyamulira zida kuti: “Solola lupanga lako+ undibaye* nalo, kuti amuna osadulidwawa+ asandipeze ndi kundibaya komanso kundizunza.” Koma womunyamulira zida uja sanafune,+ chifukwa anali kuopa kwambiri. Chotero Sauli anatenga lupanga lake ndi kuligwera.+ 2 Samueli 1:23 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 23 Sauli ndi Yonatani,+ anthu okondeka ndi osangalatsa pamene anali ndi moyo,Ngakhale pa imfa yawo sanasiyane.+Iwo anali aliwiro kuposa chiwombankhanga,+Amphamvu kuposa mikango.+ Machitidwe 13:21 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 21 Koma kuchokera pamenepo anthuwo ananena kuti akufuna mfumu.+ Chotero Mulungu anawapatsa Sauli mwana wa Kisi, munthu wa fuko la Benjamini,+ ndipo anakhala mfumu yawo kwa zaka 40.
15 Choncho anthu onse anapita ku Giligala ndipo analonga Sauli kukhala mfumu pamaso pa Yehova ku Giligalako. Kenako anapereka nsembe zachiyanjano pamaso pa Yehova+ kumeneko, ndipo Sauli pamodzi ndi amuna onse a Isiraeli anali osangalala kwambiri.+
13 Pamenepo Samueli anauza Sauli kuti: “Wachita chinthu chopusa.+ Sunatsatire lamulo+ limene Yehova Mulungu wako anakupatsa.+ Ukanatsatira lamulo limeneli, Yehova akanalimbitsa ufumu wako pa Isiraeli mpaka kalekale.
26 Samueli anamuyankha kuti: “Sindibwerera nawe chifukwa wakana mawu a Yehova, ndipo Yehova wakukana kuti upitirize kukhala mfumu ya Isiraeli.”+
23 Ndiyeno mzimu woipa wa Mulungu ukafika pa Sauli, Davide anali kutenga zeze ndi kumuimbira. Akatero, Sauli anali kupeza bwino, ndipo mzimu woipawo unali kum’chokera.+
7 Pamapeto pake, Sauli anauza atumiki ake kuti: “Ndifufuzireni mkazi waluso polankhula ndi mizimu,+ ndipo ine ndipita kukalankhula naye.” Pamenepo atumiki ake anamuuza kuti: “Ku Eni-dori alipo mkazi waluso polankhula ndi mizimu.”+
4 Kenako Sauli anauza womunyamulira zida kuti: “Solola lupanga lako+ undibaye* nalo, kuti amuna osadulidwawa+ asandipeze ndi kundibaya komanso kundizunza.” Koma womunyamulira zida uja sanafune,+ chifukwa anali kuopa kwambiri. Chotero Sauli anatenga lupanga lake ndi kuligwera.+
23 Sauli ndi Yonatani,+ anthu okondeka ndi osangalatsa pamene anali ndi moyo,Ngakhale pa imfa yawo sanasiyane.+Iwo anali aliwiro kuposa chiwombankhanga,+Amphamvu kuposa mikango.+
21 Koma kuchokera pamenepo anthuwo ananena kuti akufuna mfumu.+ Chotero Mulungu anawapatsa Sauli mwana wa Kisi, munthu wa fuko la Benjamini,+ ndipo anakhala mfumu yawo kwa zaka 40.