Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • 1 Samueli 14:49
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 49 Ana aamuna a Sauli anali Yonatani,+ Isivi ndi Malikisuwa.+ Ndipo mayina a ana ake awiri aakazi ndi awa: Woyamba kubadwa anali Merabu,+ ndipo wamng’ono anali Mikala.+

  • 1 Samueli 19:11
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 11 Kenako Sauli anatumiza amithenga+ kunyumba ya Davide kuti akaizungulire ndi kupha Davide m’mawa mwa tsiku limenelo.+ Koma Mikala mkazi wa Davide anauza Davideyo kuti: “Ngati supulumutsa moyo wako usiku uno, mawa ukhala utaphedwa.”

  • 1 Samueli 25:44
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 44 Koma Sauli anali atapereka Mikala+ mwana wake wamkazi, mkazi wake wa Davide, kwa Paliti,+ mwana wamwamuna wa Laisi wa ku Galimu.+

  • 2 Samueli 3:13
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 13 Davide anamuyankha kuti: “Chabwino! Ineyo ndichitadi nawe pangano. Koma ndikukupempha chinthu chimodzi ichi, ‘Usadzaone nkhope yanga+ pokhapokha utabweretsa Mikala,+ mwana wamkazi wa Sauli pobwera kuno.’”

  • 2 Samueli 6:16
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 16 Ndiyeno pamene likasa la Yehova linalowa mu Mzinda wa Davide, Mikala+ mwana wamkazi wa Sauli anasuzumira pawindo kuyang’ana pansi ndipo anaona Mfumu Davide akudumphadumpha ndi kuvina mozungulira pamaso pa Yehova. Pamenepo Mikala anayamba kum’peputsa+ mumtima mwake.+

  • 1 Mbiri 15:29
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 29 Ndiyeno likasa la pangano+ la Yehova litafika mu Mzinda wa Davide, Mikala+ mwana wamkazi wa Sauli anasuzumira pawindo kuyang’ana pansi, ndipo anaona Mfumu Davide akudumphadumpha ndi kusangalala.+ Pamenepo Mikala anayamba kum’peputsa+ mumtima mwake.

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena