29 Ndiyeno likasa la pangano+ la Yehova litafika mu Mzinda wa Davide, Mikala+ mwana wamkazi wa Sauli anasuzumira pawindo kuyang’ana pansi, ndipo anaona Mfumu Davide akudumphadumpha ndi kusangalala.+ Pamenepo Mikala anayamba kum’peputsa+ mumtima mwake.