18 Mmodzi mwa atumikiwo anayankha, kuti: “Inetu ndinaona luso loimba+ la mwana wa Jese wa ku Betelehemu. Iye ndi mwamuna wolimba mtima ndiponso wamphamvu,+ mwamuna wankhondo,+ wolankhula mwanzeru+ ndi wooneka bwino,+ komanso Yehova ali naye.”+
8 Mayina a amuna amphamvu+ a Davide ndi awa: Yosebu-basebete+ Mtahakemoni, mtsogoleri wa amuna atatu. Iye anatenga mkondo wake n’kupha anthu 800 ulendo umodzi.
18 Koma Abisai,+ m’bale wake wa Yowabu mwana wa Zeruya+ anali mtsogoleri wa anthu 30 amenewo. Iye ananyamula mkondo ndi kupha nawo anthu 300. Abisai anali wotchuka ngati amuna atatu aja.+