Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Deuteronomo 32:39
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 39 Onani tsopano kuti ndine Mulungu,+

      Ndipo palibe milungu ina pamodzi ndi ine.+

      Ndimapha ndiponso ndimapereka moyo.+

      Ndavulaza koopsa,+ ndipo ine ndidzachiritsa,+

      Palibe aliyense wonditsomphola m’dzanja langa.+

  • 1 Samueli 2:6
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    •  6 Yehova ndi Wakupha ndi Wosunga moyo,+

      Iye ndi Wotsitsira Kumanda,+ ndiponso Woukitsa.+

  • 2 Mafumu 4:34
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 34 Kenako anapita pabedipo ndipo anagwada n’kuweramira mwanayo.+ Anagunditsa pakamwa pake ndi pakamwa pa mwanayo. Maso ake anakhudzana ndi maso a mwanayo, manja ake anawaika pa manja a mwanayo. Anakhalabe chowerama choncho mpaka thupi la mwanayo linayamba kufunda.

  • 2 Mafumu 13:21
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 21 Tsiku lina pamene anthu anali kuika munthu m’manda, anaona gulu la achifwamba. Nthawi yomweyo iwo anaponya mtembo wa munthuyo m’manda a Elisa n’kuthawa. Mtembowo utangokhudza mafupa a Elisa, munthuyo anakhalanso wamoyo+ ndipo anaimirira.+

  • Luka 7:15
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 15 Pamenepo wakufayo anadzuka ndi kukhala tsonga, ndipo anayamba kulankhula. Kenako anam’pereka kwa mayi ake.+

  • Luka 8:55
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 55 Pamenepo mzimu wake+ unabwerera, ndipo nthawi yomweyo anadzuka.+ Ndiyeno anawauza kuti am’patse chakudya mtsikanayo.+

  • Yohane 5:28
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 28 Musadabwe nazo zimenezi, chifukwa idzafika nthawi pamene onse ali m’manda achikumbutso+ adzamva mawu ake

  • Yohane 11:44
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 44 Amene anali wakufa uja anatuluka. Mapazi ndi manja ake anali okulungidwa ndi nsalu zamaliro,+ nkhope yakenso inali yomanga ndi nsalu. Ndiyeno Yesu anawauza kuti: “M’masuleni ndi kumuleka apite.”

  • Machitidwe 9:41
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 41 Tsopano Petulo anamupatsa dzanja lake ndi kumuimiritsa.+ Atatero anaitana oyerawo ndi akazi amasiye aja, ndipo anamupereka kwa iwo ali wamoyo.+

  • Machitidwe 20:10
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 10 Koma Paulo anatsika pansi, ndipo anadziponya pa iye+ ndi kumukumbatira. Kenako ananena kuti: “Khalani chete, pakuti ali moyo tsopano.”+

  • Aroma 14:9
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 9 Ndiye chifukwa chake Khristu anafa n’kukhalanso ndi moyo,+ kuti akhale Ambuye wa akufa+ ndiponso wa amoyo.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena