Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Levitiko 17:4
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 4 koma osabwera nayo pakhomo la chihema chokumanako,+ kuti aipereke monga nsembe kwa Yehova patsogolo pa chihema cha Yehova, ameneyo adzakhala ndi mlandu wa magazi. Munthu ameneyo wakhetsa magazi, ndipo ayenera kuphedwa kuti asakhalenso pakati pa anthu amtundu wake.+

  • Levitiko 26:30
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 30 Ndipo ndidzafafaniza malo anu opatulika olambirirako+ ndi kugwetsa maguwa anu ofukizirapo zonunkhira. Ndidzaponya mitembo yanu pamwamba pa mafano anu onyansa* opanda moyowo,+ ndipo mudzakhala onyansa kwa ine.+

  • Deuteronomo 12:6
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 6 Nsembe zanu zopsereza+ ndi nsembe zina, zopereka zanu za chakhumi,*+ chopereka chochokera m’manja mwanu,+ nsembe zanu za lonjezo,+ nsembe zanu zaufulu,+ ana oyamba kubadwa a ng’ombe ndi a nkhosa zanu,+ zonsezi muzidzazibweretsa kumalo amenewo.

  • 1 Mafumu 15:14
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 14 Koma iye sanachotse+ malo okwezeka.+ Komabe, Asa anatumikira Yehova ndi mtima wathunthu masiku ake onse.+

  • 1 Mafumu 22:43
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 43 Yehosafati anayenda m’njira zonse za Asa bambo ake. Sanapatuke panjirazo, ndipo anapitiriza kuchita zoyenera pamaso pa Yehova.+ Koma sanachotse malo okwezeka. Anthu anali kufukizabe ndi kupereka nsembe yautsi m’malo okwezekawo.+

  • 2 Mbiri 33:17
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 17 Komabe anthu anali kuperekabe nsembe m’malo okwezeka,+ kungoti anali kuzipereka kwa Yehova Mulungu wawo.

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena