Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Numeri 35:33
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 33 “‘Musadetse dziko+ limene mukukhalamo, chifukwa magazi ndiwo amadetsa dziko. Ndipo dziko lodetsedwa ndi magazi silingayeretsedwe mwa njira ina, koma ndi magazi a munthu amene anakhetsa magaziyo.+

  • Deuteronomo 19:10
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 10 kuti musakhetse magazi a munthu wosalakwa+ pakati pa dziko lanu limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani monga cholowa, kotero kuti musakhale ndi mlandu wa magazi.+

  • 2 Mafumu 21:16
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 16 Manase anakhetsanso magazi osalakwa ochuluka zedi,+ mpaka magaziwo anadzaza nawo Yerusalemu kuyambira koyambirira mpaka kumapeto, kuwonjezera pa tchimo lake limene anachimwitsa nalo Yuda mwa kuchita zoipa pamaso pa Yehova.+

  • Salimo 106:38
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 38 Choncho anali kukhetsa magazi a anthu osalakwa,+

      Magazi a ana awo aamuna ndi a ana awo aakazi,

      Amene anawapereka nsembe kwa mafano a ku Kanani.+

      Ndipo dzikolo linaipa ndi magazi amene iwo anakhetsa.+

  • Yeremiya 2:34
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 34 Komanso, pazovala zako papezeka madontho a magazi a anthu+ osauka osalakwa.+ Madontho a magaziwo sindinawapeze panyumba, ngati kuti anali kuthyola nyumbayo, koma ndawapeza pazovala zako zonse.+

  • Yeremiya 19:4
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 4 Zidzatero chifukwa andisiya+ ndiponso achititsa kuti malo ano ndisawazindikire.+ Iwo amaperekanso nsembe zautsi kwa milungu ina imene sanali kuidziwa,+ iwowo, makolo awo ndi mafumu a Yuda, ndipo adzaza malo ano ndi magazi a anthu osalakwa.+

  • Yeremiya 22:17
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 17 ‘Ndithudi, maso ako ndi mtima wako sizikulakalaka china chilichonse koma phindu lachinyengo,+ anthu osalakwa kuti ukhetse magazi awo+ komanso kuba mwachinyengo ndi kulanda.’

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena