Oweruza 6:31 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 31 Koma Yowasi+ anauza onse amene anamuukirawo kuti:+ “Kodi inu mungaweruzire Baala mlandu kuti mum’pulumutse? Aliyense womuweruzira mlandu ayenera kuphedwa m’mawa womwe uno.+ Ngati Baalayo ndi Mulungu,+ adziweruzire yekha mlanduwu,+ chifukwa wina wake wagwetsa guwa lake lansembe.” 1 Samueli 24:15 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 15 Yehova akhale woweruza, ndipo aweruze pakati pa ine ndi inu. Iye adzandiweruzira mlanduwu+ ndi kuchitapo kanthu kuti andimasule m’manja mwanu.” Salimo 35:1 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 35 Weruzani mlandu wanga inu Yehova, motsutsana ndi adani anga.+Menyani nkhondo ndi kugonjetsa amene akumenyana ndi ine.+ Salimo 43:1 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 43 Ndiweruzeni+ inu Mulungu,Weruzani mlandu wanga+ motsutsana ndi mtundu wosakhulupirika.Ndipulumutseni kwa munthu wachinyengo ndi wochita zosalungama.+ Miyambo 22:23 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 23 Pakuti Yehova adzawateteza pa mlandu wawo,+ ndipo adzalanda moyo wa amene akuwabera.+ Miyambo 23:11 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 11 Pakuti Wowawombola ndi wamphamvu, ndipo adzawateteza pa mlandu wawo ndi iwe.+ Yeremiya 50:34 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 34 Wowawombola ndi wamphamvu,+ dzina lake ndi Yehova wa makamu.+ Iye sadzalephera kuwaweruzira mlandu wawo+ kuti apumitse dziko lawo+ ndiponso kusokoneza mtendere wa anthu okhala m’Babulo.”+ Maliro 3:59 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 59 Inu Yehova, mwaona zoipa zimene andichitira.+ Chonde, ndiweruzireni mlandu wanga.+ Mika 7:9 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 9 Mkwiyo waukulu wa Yehova ndiupirira chifukwa ndamuchimwira.+ Ndiupirirabe kufikira ataweruza mlandu wanga mondikomera ndi kundichitira chilungamo.+ Iye adzandipititsa pamalo owala ndipo ndidzaona kulungama kwake.+
31 Koma Yowasi+ anauza onse amene anamuukirawo kuti:+ “Kodi inu mungaweruzire Baala mlandu kuti mum’pulumutse? Aliyense womuweruzira mlandu ayenera kuphedwa m’mawa womwe uno.+ Ngati Baalayo ndi Mulungu,+ adziweruzire yekha mlanduwu,+ chifukwa wina wake wagwetsa guwa lake lansembe.”
15 Yehova akhale woweruza, ndipo aweruze pakati pa ine ndi inu. Iye adzandiweruzira mlanduwu+ ndi kuchitapo kanthu kuti andimasule m’manja mwanu.”
35 Weruzani mlandu wanga inu Yehova, motsutsana ndi adani anga.+Menyani nkhondo ndi kugonjetsa amene akumenyana ndi ine.+
43 Ndiweruzeni+ inu Mulungu,Weruzani mlandu wanga+ motsutsana ndi mtundu wosakhulupirika.Ndipulumutseni kwa munthu wachinyengo ndi wochita zosalungama.+
34 Wowawombola ndi wamphamvu,+ dzina lake ndi Yehova wa makamu.+ Iye sadzalephera kuwaweruzira mlandu wawo+ kuti apumitse dziko lawo+ ndiponso kusokoneza mtendere wa anthu okhala m’Babulo.”+
9 Mkwiyo waukulu wa Yehova ndiupirira chifukwa ndamuchimwira.+ Ndiupirirabe kufikira ataweruza mlandu wanga mondikomera ndi kundichitira chilungamo.+ Iye adzandipititsa pamalo owala ndipo ndidzaona kulungama kwake.+