-
2 Samueli 20:22Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
22 Nthawi yomweyo, mkaziyo anapita mwa nzeru+ zake kwa anthu onse, ndipo anthuwo anadula mutu wa Sheba mwana wa Bikiri ndi kuuponya kwa Yowabu. Zitatero, Yowabu analiza lipenga la nyanga ya nkhosa+ moti anthu onse anabalalika kuchoka kumzindawo ndi kupita kwawo. Yowabu nayenso anabwerera ku Yerusalemu kwa mfumu.
-
-
Esitere 7:9Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
9 Haribona,+ mmodzi mwa nduna za panyumba ya mfumu+ amene anali pamaso pa mfumu anati: “Palinso mtengo+ umene Hamani anapangira Moredekai, amene analankhula zabwino za mfumu.+ Mtengowu uli m’nyumba ya Hamani ndipo ndi wotalika mikono 50.” Pamenepo mfumu inati: “Amuna inu, kam’pachikeni pamtengo umenewo.”+
-