1 Mbiri 17:11 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 11 “‘“Masiku ako akadzakwana kuti ukakhale pamodzi ndi makolo ako,+ pamenepo ndithu ndidzautsa mbewu yako yobwera pambuyo pako,+ imene idzakhala mmodzi wa ana ako, ndipo ndidzakhazikitsadi ufumu wake.+ Yesaya 4:2 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 2 M’tsiku limenelo, chinthu chimene Yehova adzachiphukitse+ chidzakhala chokongoletsera ndi chaulemerero.+ Zipatso za m’dzikolo zidzakhala zonyaditsa+ ndi zokongola kwa Aisiraeli amene adzapulumuke.+ Yesaya 11:1 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 11 Nthambi+ idzatuluka pachitsa cha Jese,+ ndipo mphukira+ yotuluka pamizu yake idzakhala yobereka zipatso.+ Yesaya 53:2 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 2 Iye adzaphuka ngati nthambi+ pamaso pa winawake, ndiponso ngati muzu m’dziko lopanda madzi. Alibe maonekedwe alionse apamwamba kapena okongola,+ ndipo maonekedwe ake si osiririka m’maso mwathu.+ Yeremiya 23:5 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 5 “Taonani! Masiku adzafika,” watero Yehova, “ndipo Davide ndidzamuutsira mphukira yolungama.+ Ndithudi mfumu idzalamulira+ m’dzikoli ndi kuchita zinthu mozindikira, motsatira malamulo komanso mwachilungamo.+ Zekariya 3:8 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 8 “‘Tamvera iwe Yoswa mkulu wa ansembe ndi anzako amene akhala pansi pamaso pako, pakuti iwo ndi amuna amene ali ngati zizindikiro zolosera zam’tsogolo.+ Ine ndibweretsa mtumiki wanga+ dzina lake Mphukira.+ Zekariya 6:12 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 12 Ndiyeno udzamuuze kuti,“‘Yehova wa makamu wanena kuti: “Munthu uyu+ dzina lake ndi Mphukira.+ Adzaphuka pamalo ake ndipo adzamanga kachisi wa Yehova.+ Chivumbulutso 22:16 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 16 “‘Ine Yesu, ndinatumiza mngelo wanga kudzachitira umboni zinthu izi kwa inu, kuti zithandize mipingo. Ine ndine muzu+ ndi mbadwa+ ya Davide. Ndinenso nthanda yonyezimira.’”+
11 “‘“Masiku ako akadzakwana kuti ukakhale pamodzi ndi makolo ako,+ pamenepo ndithu ndidzautsa mbewu yako yobwera pambuyo pako,+ imene idzakhala mmodzi wa ana ako, ndipo ndidzakhazikitsadi ufumu wake.+
2 M’tsiku limenelo, chinthu chimene Yehova adzachiphukitse+ chidzakhala chokongoletsera ndi chaulemerero.+ Zipatso za m’dzikolo zidzakhala zonyaditsa+ ndi zokongola kwa Aisiraeli amene adzapulumuke.+
11 Nthambi+ idzatuluka pachitsa cha Jese,+ ndipo mphukira+ yotuluka pamizu yake idzakhala yobereka zipatso.+
2 Iye adzaphuka ngati nthambi+ pamaso pa winawake, ndiponso ngati muzu m’dziko lopanda madzi. Alibe maonekedwe alionse apamwamba kapena okongola,+ ndipo maonekedwe ake si osiririka m’maso mwathu.+
5 “Taonani! Masiku adzafika,” watero Yehova, “ndipo Davide ndidzamuutsira mphukira yolungama.+ Ndithudi mfumu idzalamulira+ m’dzikoli ndi kuchita zinthu mozindikira, motsatira malamulo komanso mwachilungamo.+
8 “‘Tamvera iwe Yoswa mkulu wa ansembe ndi anzako amene akhala pansi pamaso pako, pakuti iwo ndi amuna amene ali ngati zizindikiro zolosera zam’tsogolo.+ Ine ndibweretsa mtumiki wanga+ dzina lake Mphukira.+
12 Ndiyeno udzamuuze kuti,“‘Yehova wa makamu wanena kuti: “Munthu uyu+ dzina lake ndi Mphukira.+ Adzaphuka pamalo ake ndipo adzamanga kachisi wa Yehova.+
16 “‘Ine Yesu, ndinatumiza mngelo wanga kudzachitira umboni zinthu izi kwa inu, kuti zithandize mipingo. Ine ndine muzu+ ndi mbadwa+ ya Davide. Ndinenso nthanda yonyezimira.’”+