Salimo 2:6 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 6 Ndipo adzanena kuti: “Inetu ndakhazika mfumu yanga+Pa Ziyoni,+ phiri langa lopatulika.”+ Salimo 8:6 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 6 Munamupatsa mphamvu kuti alamulire ntchito za manja anu.+Mwaika zonse pansi pa mapazi ake:+ Salimo 89:27 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 27 Inenso ndidzamuika kukhala mwana woyamba kubadwa,+Ndiponso mfumu yaikulu pa mafumu onse a padziko lapansi.+ Salimo 110:2 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 2 Yehova adzatambasula ndodo+ yako yachifumu yamphamvu kuchokera m’Ziyoni+ ndi kunena kuti:“Pita ukagonjetse anthu pakati pa adani ako.”+ Yesaya 9:6 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 6 Pakuti kwa ife kwabadwa mwana.+ Ife tapatsidwa mwana wamwamuna,+ ndipo paphewa pake padzakhala ulamuliro.+ Iye adzapatsidwa dzina lakuti Mlangizi Wodabwitsa,+ Mulungu Wamphamvu,+ Atate Wosatha,+ Kalonga Wamtendere.+ Mateyu 28:18 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 18 Tsopano Yesu anayandikira ndi kulankhula nawo kuti: “Ulamuliro wonse+ waperekedwa kwa ine kumwamba ndi padziko lapansi. Luka 10:22 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 22 Atate wanga wapereka+ zinthu zonse kwa ine, ndipo palibe amene akum’dziwa bwino Mwana koma Atate okha. Komanso Atatewo+ palibe amene akuwadziwa bwino koma Mwana+ yekha ndiponso amene Mwanayo wakonda kuwaululira za Atatewo.” 1 Akorinto 15:25 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 25 Pakuti ayenera kulamulira monga mfumu kufikira Mulungu ataika adani onse pansi pa mapazi+ ake. Aefeso 1:22 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 22 Mulungu anaikanso zinthu zonse pansi pa mapazi a iyeyo,+ ndipo anamuika mutu wa zinthu zonse+ chifukwa cha mpingo, Chivumbulutso 3:21 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 21 Wopambana pa nkhondo+ ndidzamulola kukhala nane pampando wanga wachifumu,+ monga mmene ine ndinakhalira+ ndi Atate wanga pampando wawo wachifumu+ nditapambana pa nkhondo.
27 Inenso ndidzamuika kukhala mwana woyamba kubadwa,+Ndiponso mfumu yaikulu pa mafumu onse a padziko lapansi.+
2 Yehova adzatambasula ndodo+ yako yachifumu yamphamvu kuchokera m’Ziyoni+ ndi kunena kuti:“Pita ukagonjetse anthu pakati pa adani ako.”+
6 Pakuti kwa ife kwabadwa mwana.+ Ife tapatsidwa mwana wamwamuna,+ ndipo paphewa pake padzakhala ulamuliro.+ Iye adzapatsidwa dzina lakuti Mlangizi Wodabwitsa,+ Mulungu Wamphamvu,+ Atate Wosatha,+ Kalonga Wamtendere.+
18 Tsopano Yesu anayandikira ndi kulankhula nawo kuti: “Ulamuliro wonse+ waperekedwa kwa ine kumwamba ndi padziko lapansi.
22 Atate wanga wapereka+ zinthu zonse kwa ine, ndipo palibe amene akum’dziwa bwino Mwana koma Atate okha. Komanso Atatewo+ palibe amene akuwadziwa bwino koma Mwana+ yekha ndiponso amene Mwanayo wakonda kuwaululira za Atatewo.”
22 Mulungu anaikanso zinthu zonse pansi pa mapazi a iyeyo,+ ndipo anamuika mutu wa zinthu zonse+ chifukwa cha mpingo,
21 Wopambana pa nkhondo+ ndidzamulola kukhala nane pampando wanga wachifumu,+ monga mmene ine ndinakhalira+ ndi Atate wanga pampando wawo wachifumu+ nditapambana pa nkhondo.