16 Komanso muzichita chikondwerero cha zokolola, chokondwerera zipatso za ntchito ya manja anu zoyamba kucha+ zimene munabzala m’munda.+ Muzichitanso chikondwerero cha kututa kumapeto kwa chaka, pamene mututa zipatso za manja anu, zam’munda.+
12 “‘Pa tsiku la 15 la mwezi wa 7,+ muzichita msonkhano wopatulika.+ Musamagwire ntchito yolemetsa yamtundu uliwonse.+ Muzichita chikondwerero kwa Yehova masiku 7.+
14 Pamenepo anapeza kuti m’chilamulo chimene Yehova anawapatsa kudzera mwa Mose+ analembamo kuti ana a Isiraeli azikhala m’misasa+ pa nthawi ya chikondwerero m’mwezi wa 7.+
16 “Aliyense wotsala mwa anthu a mitundu yonse amene akubwera kudzamenyana ndi Yerusalemu,+ azidzapita kukagwadira Mfumu,+ Yehova wa makamu,+ chaka ndi chaka,+ ndi kukachita nawo chikondwerero cha misasa.+