-
2 Mbiri 7:6Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
6 Ansembe+ anali ataimirira m’malo awo a ntchito pamodzi ndi Alevi,+ onse atanyamula zipangizo zoimbira+ Yehova nyimbo zimene Davide+ mfumu anapanga kuti aziyamikira Yehova. Aleviwo anali kunena kuti “pakuti kukoma mtima kwake kosatha kudzakhala mpaka kalekale.” Iwo ankanena zimenezi paliponse pamene Davide akanatamanda Mulungu kudzera mwa iwo. Ansembe anali kuimba malipenga+ mokweza patsogolo pawo, Aisiraeli onse ataimirira.
-
-
Ezara 3:10Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
10 Tsopano anthu amene anali kugwira ntchito yomanga nyumbayo anamaliza kumanga maziko+ a kachisi wa Yehova. Atatero, ansembe ovala zovala zaunsembe+ omwe ananyamula malipenga,+ ndiponso Alevi ana a Asafu+ omwe ananyamula zinganga,+ anaimirira kuti atamande Yehova motsatira dongosolo+ limene Davide mfumu ya Isiraeli anakhazikitsa.
-