Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • 1 Mbiri 15:28
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 28 Aisiraeli onse anali kupita ndi likasa la pangano la Yehova akufuula mokondwera,+ ndiponso akuliza nyanga za nkhosa+ ndi malipenga.+ Iwo anali kuimbanso mokweza zinganga,+ zoimbira za zingwe, ndi azeze.+

  • 2 Mbiri 5:12
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 12 Ndipo Alevi+ oimba a m’gulu la Asafu,+ Hemani,+ Yedutuni,+ ana awo ndi abale awo, onsewa atavala zovala zabwino kwambiri atanyamula zinganga,+ zoimbira za zingwe+ ndi azeze,+ anaimirira kum’mawa kwa guwa lansembe pamodzi ndi ansembe okwanira 120 oimba malipenga.+

  • 2 Mbiri 7:6
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 6 Ansembe+ anali ataimirira m’malo awo a ntchito pamodzi ndi Alevi,+ onse atanyamula zipangizo zoimbira+ Yehova nyimbo zimene Davide+ mfumu anapanga kuti aziyamikira Yehova. Aleviwo anali kunena kuti “pakuti kukoma mtima kwake kosatha kudzakhala mpaka kalekale.” Iwo ankanena zimenezi paliponse pamene Davide akanatamanda Mulungu kudzera mwa iwo. Ansembe anali kuimba malipenga+ mokweza patsogolo pawo, Aisiraeli onse ataimirira.

  • Ezara 3:10
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 10 Tsopano anthu amene anali kugwira ntchito yomanga nyumbayo anamaliza kumanga maziko+ a kachisi wa Yehova. Atatero, ansembe ovala zovala zaunsembe+ omwe ananyamula malipenga,+ ndiponso Alevi ana a Asafu+ omwe ananyamula zinganga,+ anaimirira kuti atamande Yehova motsatira dongosolo+ limene Davide mfumu ya Isiraeli anakhazikitsa.

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena