Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • 1 Mbiri 29:10
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 10 Kenako Davide anatamanda+ Yehova pamaso pa mpingo wonse,+ kuti: “Mudalitsike+ inu Yehova Mulungu wa Isiraeli+ atate wathu, kuyambira kalekale mpaka kalekale.

  • Nehemiya 9:5
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 5 Choncho Yesuwa, Kadimiyeli, Bani, Hasabineya, Serebiya, Hodiya, Sebaniya ndi Petahiya, omwe anali Alevi, anati: “Dzukani, tamandani+ Yehova Mulungu wanu kuyambira kalekale mpaka kalekale.*+ Inu Mulungu wathu, anthuwa atamande dzina lanu laulemerero,+ lokwezeka kuposa dalitso ndi chitamando chilichonse.

  • Salimo 34:1
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 34 Ndidzatamanda Yehova nthawi zonse.+

      Ndidzamutamanda ndi pakamwa panga mosalekeza.+

  • Salimo 72:18
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 18 Adalitsike Yehova Mulungu, Mulungu wa Isiraeli,+

      Iye yekha amene akuchita ntchito zodabwitsa.+

  • Danieli 4:34
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 34 “Pamapeto pa masiku amenewa,+ ine Nebukadinezara ndinakweza maso anga kumwamba+ ndipo nzeru zanga zinayamba kubwerera. Ndinatamanda Wam’mwambamwamba+ ndipo amene adzakhalapo mpaka kalekale ndinamutamanda ndi kumulemekeza,+ chifukwa ulamuliro wake udzakhalapo mpaka kalekale ndipo ufumu wake udzakhalapo ku mibadwomibadwo.+

  • Aefeso 1:3
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 3 Atamandike Mulungu, Atate wa Ambuye wathu Yesu Khristu,+ pakuti watidalitsa+ ndi dalitso lililonse lauzimu m’malo akumwamba+ mogwirizana ndi Khristu.

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena