Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Oweruza 1:27
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 27 Manase+ sanatenge mzinda wa Beti-seani+ ndi midzi yake yozungulira, Taanaki+ ndi midzi yake yozungulira, ndipo sanapitikitse anthu okhala mumzinda wa Dori+ ndi midzi yake yozungulira, anthu a mumzinda wa Ibuleamu+ ndi midzi yake yozungulira, ndi anthu okhala mumzinda wa Megido+ ndi midzi yake yozungulira. Akananiwo anakakamirabe kukhala m’dziko limeneli.+

  • Oweruza 5:19
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 19 Mafumu anabwera ndi kumenya nkhondo.

      Pamenepo mafumu a Kanani anamenya nkhondo,+

      Anamenya nkhondo ku Taanaki,+ pafupi ndi madzi a ku Megido.+

      Iwo sanapezepo phindu la siliva.+

  • 1 Mafumu 4:12
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 12 Baana mwana wa Ahiludi, ku Taanaki+ ndi ku Megido+ ndi ku Beti-seani+ konse, pafupi ndi Zeretani+ kumunsi kwa Yezereeli,+ kuchokera ku Beti-seani kukafika ku Abele-mehola+ mpaka kuchigawo cha Yokimeamu,+

  • 2 Mafumu 9:27
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 27 Ahaziya+ mfumu ya Yuda, anaona zonsezo moti anayamba kuthawa kudzera njira ya kumunda.*+ (Pambuyo pake Yehu anayamba kum’tsatira, ndipo anati: “Ameneyonso m’kantheni!” Choncho anam’kanthadi ali m’galeta lake pamene anali kuthawira ku Guru, kufupi ndi ku Ibuleamu.+ Iye anapitirizabe kuthawa mpaka ku Megido+ kumene anakafera.+

  • 2 Mafumu 23:30
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 30 Choncho atumiki ake ananyamula mtembo wake pagaleta kuchokera ku Megido n’kupita nawo ku Yerusalemu+ kumene anakauika m’manda ake. Kenako anthu a m’dzikolo anatenga Yehoahazi+ mwana wa Yosiya n’kumudzoza ndi kumulonga ufumu m’malo mwa bambo ake.

  • Zekariya 12:11
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 11 Pa tsiku limenelo, anthu adzalira kwambiri mu Yerusalemu ngati mmene analirira ku Hadadirimoni, m’chigwa cha Megido.+

  • Chivumbulutso 16:16
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 16 Ndipo anawasonkhanitsa pamodzi, kumalo amene m’Chiheberi amatchedwa Haramagedo.*+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena