Salimo 14:4 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 4 Kodi palibe aliyense wozindikira mwa anthu ochita zopweteka anzawowa,+Amene akudya anthu anga ngati chakudya?+Iwo sanaitane pa Yehova.+ Miyambo 22:16 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 16 Amene amabera mwachinyengo munthu wonyozeka kuti apeze zinthu zambiri,+ komanso wopereka mphatso kwa munthu wolemera, ndithu adzasauka.+ Yesaya 32:7 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 7 Munthu wakhalidwe loipayo, njira zake n’zoipa.+ Iye amakonza zochita khalidwe lotayirira,+ n’cholinga choti apweteke anthu ozunzika pogwiritsa ntchito mawu abodza,+ ngakhale pamene munthu wosauka akunena zoona. Mika 3:3 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 3 Mwadya mnofu wa anthu anga+ ndipo mwasenda khungu lawo. Mwaswa mafupa awo kukhala zidutswazidutswa. Mwawaphwanyaphwanya ngati mafupa ndi mnofu zimene zili mumphika wakukamwa kwakukulu komanso ngati nyama imene ili mumphika.+ Habakuku 3:14 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 14 Munabaya*+ mitu ya asilikali ake ndi zida zake zomwe, pamene iwo anali kubwera ngati mphepo yamkuntho kuti adzandimwaze.+ Kukondwera kwawo chifukwa cha tsoka langa kunali ngati kwa anthu amene akonzeka kuti ameze munthu wosautsidwa m’malo obisalamo.+ Maliko 12:40 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 40 Iwo ndi amene amadyerera nyumba+ za akazi amasiye, ndipo mwachiphamaso amapereka mapemphero ataliatali. Anthu amenewa adzalandira chiweruzo champhamvu.”+ Yakobo 5:4 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 4 Tamverani! Malipiro a anthu amene anagwira ntchito+ yokolola m’minda yanu, amene inu simunapereke,+ akufuula ndipo kufuula kwa okololawo kofuna thandizo+ kwafika m’makutu+ a Yehova wa makamu.
4 Kodi palibe aliyense wozindikira mwa anthu ochita zopweteka anzawowa,+Amene akudya anthu anga ngati chakudya?+Iwo sanaitane pa Yehova.+
16 Amene amabera mwachinyengo munthu wonyozeka kuti apeze zinthu zambiri,+ komanso wopereka mphatso kwa munthu wolemera, ndithu adzasauka.+
7 Munthu wakhalidwe loipayo, njira zake n’zoipa.+ Iye amakonza zochita khalidwe lotayirira,+ n’cholinga choti apweteke anthu ozunzika pogwiritsa ntchito mawu abodza,+ ngakhale pamene munthu wosauka akunena zoona.
3 Mwadya mnofu wa anthu anga+ ndipo mwasenda khungu lawo. Mwaswa mafupa awo kukhala zidutswazidutswa. Mwawaphwanyaphwanya ngati mafupa ndi mnofu zimene zili mumphika wakukamwa kwakukulu komanso ngati nyama imene ili mumphika.+
14 Munabaya*+ mitu ya asilikali ake ndi zida zake zomwe, pamene iwo anali kubwera ngati mphepo yamkuntho kuti adzandimwaze.+ Kukondwera kwawo chifukwa cha tsoka langa kunali ngati kwa anthu amene akonzeka kuti ameze munthu wosautsidwa m’malo obisalamo.+
40 Iwo ndi amene amadyerera nyumba+ za akazi amasiye, ndipo mwachiphamaso amapereka mapemphero ataliatali. Anthu amenewa adzalandira chiweruzo champhamvu.”+
4 Tamverani! Malipiro a anthu amene anagwira ntchito+ yokolola m’minda yanu, amene inu simunapereke,+ akufuula ndipo kufuula kwa okololawo kofuna thandizo+ kwafika m’makutu+ a Yehova wa makamu.