Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Oweruza 3:7
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 7 Chotero ana a Isiraeli anachita zoipa pamaso pa Yehova, ndipo anaiwala Yehova Mulungu wawo,+ moti anayamba kutumikira Abaala+ ndi mizati yopatulika.+

  • 1 Mafumu 14:23
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 23 Ndipo nawonso anapitiriza kudzimangira malo okwezeka,+ zipilala zopatulika,+ ndi mizati yopatulika+ pamwamba pa phiri lililonse lalitali,+ ndiponso pansi pa mtengo uliwonse waukulu wa masamba obiriwira.+

  • 2 Mafumu 16:4
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 4 Ahazi ankafukiza ndi kupereka nsembe yautsi pamalo okwezeka,+ pamapiri,+ ndi pansi pa mtengo uliwonse waukulu wa masamba obiriwira.+

  • 2 Mbiri 24:18
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 18 M’kupita kwa nthawi iwo anasiya nyumba ya Yehova Mulungu wa makolo awo n’kuyamba kutumikira mizati yopatulika+ ndiponso mafano.+ Chotero mkwiyo wa Mulungu unagwera Yuda ndi Yerusalemu chifukwa cha kupalamula kwawoko.+

  • 2 Mbiri 33:3
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 3 Choncho iye anamanganso malo okwezeka+ amene Hezekiya bambo ake anagwetsa.+ Anamanga maguwa ansembe+ a Abaala+ n’kumanga mizati yopatulika,+ ndipo anayamba kugwadira+ khamu lonse la zinthu zakuthambo,+ n’kumazitumikira.+

  • Salimo 78:58
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 58 Iwo anapitiriza kumukhumudwitsa ndi malo awo okwezeka,+

      Ndipo anamuchititsa nsanje ndi zifaniziro zawo zogoba.+

  • Yesaya 1:29
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 29 Pakuti anthu adzachita manyazi ndi mitengo ikuluikulu imene inu munali kuilakalaka,+ ndipo mudzagwetsa nkhope zanu chifukwa cha minda imene mwasankha.+

  • Yeremiya 2:20
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 20 “‘Ine ndinaphwanya goli lako kukhala zidutswazidutswa kalekale.+ Ndinadula zingwe zimene anakumanga nazo. Koma iwe unati: “Sindikutumikirani,” ndipo unagona motangadza+ paphiri lililonse lalitali ndi pansi pa mtengo uliwonse waukulu wa masamba ambiri obiriwira+ n’kumachita uhule+ pamenepo.

  • Ezekieli 6:13
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 13 Iwo adzadziwa kuti ine ndine Yehova.+ Adzadziwa zimenezi mitembo ya anthu awo ikadzakhala pakati pa mafano awo onyansa+ kuzungulira maguwa awo onse ansembe,+ paphiri lililonse lalitali,+ pansonga zonse za mapiri,+ pansi pa mtengo uliwonse waukulu wamasamba obiriwira,+ ndiponso pansi pa mtengo uliwonse waukulu wanthambi zambiri.+ Amenewa ndiwo malo amene anali kuperekerapo nsembe zafungo lokhazika mtima pansi kwa mafano awo onse onyansa.+

  • Ezekieli 20:28
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 28 Komabe ine ndinawalowetsa m’dziko+ limene ndinawalumbirira nditakweza dzanja langa kuti ndidzawapatsa.+ Koma ataona phiri lililonse lalitali+ ndi mtengo uliwonse wanthambi zambiri, anayamba kupereka nsembe zawo pamenepo+ ndi zopereka zawo zochititsa mseru. Analinso kufukiza nsembe zafungo lokhazika mtima pansi+ ndi kuthira nsembe zawo zachakumwa pamalo amenewo.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena