Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Deuteronomo 5
  • Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

Zimene Zili Mʼbuku la Deuteronomo

      • Yehova anachita pangano ku Horebe (1-5)

      • Anabwereza kuwauza Malamulo Khumi (6-22)

      • Anthu anachita mantha paphiri la Sinai (23-33)

Deuteronomo 5:2

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Eks 19:5; Ahe 9:19, 20

Deuteronomo 5:4

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Eks 19:9, 18; Mac 7:38

Deuteronomo 5:5

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Eks 20:19; Aga 3:19
  • +Eks 19:16

Deuteronomo 5:6

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Eks 13:3; 20:2

Deuteronomo 5:7

Mawu a M'munsi

  • *

    Kapena kuti, “motsutsana ndi ine.” Mʼchilankhulo choyambirira, “motsutsana ndi nkhope yanga.”

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Eks 20:3-6; 2Mf 17:35

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Nsanja ya Olonda,

    3/1/2012, tsa. 23

Deuteronomo 5:8

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Le 26:1; De 4:15, 16, 23; 27:15; Mac 17:29

Deuteronomo 5:9

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Eks 23:24; 1Ak 10:14
  • +Eks 34:14; De 4:24; Yes 42:8; Mt 4:10
  • +Eks 34:6, 7

Deuteronomo 5:10

Mawu a M'munsi

  • *

    Kapena kuti, “kukoma mtima kosatha.”

Deuteronomo 5:11

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Eks 22:28; Le 19:12
  • +Eks 20:7; Le 24:16

Deuteronomo 5:12

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Eks 16:23; 20:8-10; 31:13

Deuteronomo 5:13

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Eks 34:21

Deuteronomo 5:14

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Eks 16:29
  • +Ne 13:15
  • +Eks 23:12
  • +De 10:17; Aef 6:9

Deuteronomo 5:15

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Eks 6:6; De 4:34

Deuteronomo 5:16

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Eks 21:15; Le 19:3; De 27:16; Miy 1:8; Mko 7:10
  • +Eks 20:12; Aef 6:2, 3

Deuteronomo 5:17

Mawu a M'munsi

  • *

    Kupha uku ndi kupha munthu mwachiwembu osati mwalamulo.

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Ge 9:6; Eks 20:13; Nu 35:20, 21; Mt 5:21; Aro 13:9

Deuteronomo 5:18

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Eks 20:14; 1Ak 6:18; Ahe 13:4

Deuteronomo 5:19

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Eks 20:15; Le 19:11; Miy 30:8, 9; 1Ak 6:10; Aef 4:28

Deuteronomo 5:20

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Eks 20:16; 23:1; Le 19:16; De 19:16-19; Miy 6:16, 19; 19:5

Deuteronomo 5:21

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Mt 5:28
  • +Eks 20:17; Lu 12:15; Aro 7:7

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Nsanja ya Olonda (Yophunzira),

    2/2019, ptsa. 21-22

    Nsanja ya Olonda,

    5/15/2012, tsa. 7

Deuteronomo 5:22

Mawu a M'munsi

  • *

    Mʼchilankhulo choyambirira, “mawu.”

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Eks 19:9, 18
  • +Eks 24:12; 31:18; De 4:12, 13

Deuteronomo 5:23

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Eks 20:18; Ahe 12:18, 19

Deuteronomo 5:24

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Eks 24:17
  • +De 4:33, 36

Deuteronomo 5:27

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Eks 20:19; Ahe 12:18, 19

Deuteronomo 5:28

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +De 18:16, 17

Deuteronomo 5:29

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +De 10:12; Yob 28:28; Miy 1:7; Mt 10:28; 1Pe 2:17
  • +Miy 4:4; 7:2; Mla 12:13; Yes 48:18; 1Yo 5:3
  • +Sl 19:8, 11; Yak 1:25

Deuteronomo 5:32

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +De 6:3, 25; 8:1
  • +De 12:32; Yos 1:7, 8

Deuteronomo 5:33

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +De 10:12
  • +De 4:40; 12:28; Aro 10:5

Mabaibulo Ena

Dinani pa nambala ya vesi kuti muone mavesi a m'Baibulo lina ofanana ndi vesilo.

Malemba Ena

Deut. 5:2Eks 19:5; Ahe 9:19, 20
Deut. 5:4Eks 19:9, 18; Mac 7:38
Deut. 5:5Eks 20:19; Aga 3:19
Deut. 5:5Eks 19:16
Deut. 5:6Eks 13:3; 20:2
Deut. 5:7Eks 20:3-6; 2Mf 17:35
Deut. 5:8Le 26:1; De 4:15, 16, 23; 27:15; Mac 17:29
Deut. 5:9Eks 23:24; 1Ak 10:14
Deut. 5:9Eks 34:14; De 4:24; Yes 42:8; Mt 4:10
Deut. 5:9Eks 34:6, 7
Deut. 5:11Eks 22:28; Le 19:12
Deut. 5:11Eks 20:7; Le 24:16
Deut. 5:12Eks 16:23; 20:8-10; 31:13
Deut. 5:13Eks 34:21
Deut. 5:14Eks 16:29
Deut. 5:14Ne 13:15
Deut. 5:14Eks 23:12
Deut. 5:14De 10:17; Aef 6:9
Deut. 5:15Eks 6:6; De 4:34
Deut. 5:16Eks 21:15; Le 19:3; De 27:16; Miy 1:8; Mko 7:10
Deut. 5:16Eks 20:12; Aef 6:2, 3
Deut. 5:17Ge 9:6; Eks 20:13; Nu 35:20, 21; Mt 5:21; Aro 13:9
Deut. 5:18Eks 20:14; 1Ak 6:18; Ahe 13:4
Deut. 5:19Eks 20:15; Le 19:11; Miy 30:8, 9; 1Ak 6:10; Aef 4:28
Deut. 5:20Eks 20:16; 23:1; Le 19:16; De 19:16-19; Miy 6:16, 19; 19:5
Deut. 5:21Mt 5:28
Deut. 5:21Eks 20:17; Lu 12:15; Aro 7:7
Deut. 5:22Eks 19:9, 18
Deut. 5:22Eks 24:12; 31:18; De 4:12, 13
Deut. 5:23Eks 20:18; Ahe 12:18, 19
Deut. 5:24Eks 24:17
Deut. 5:24De 4:33, 36
Deut. 5:27Eks 20:19; Ahe 12:18, 19
Deut. 5:28De 18:16, 17
Deut. 5:29De 10:12; Yob 28:28; Miy 1:7; Mt 10:28; 1Pe 2:17
Deut. 5:29Miy 4:4; 7:2; Mla 12:13; Yes 48:18; 1Yo 5:3
Deut. 5:29Sl 19:8, 11; Yak 1:25
Deut. 5:32De 6:3, 25; 8:1
Deut. 5:32De 12:32; Yos 1:7, 8
Deut. 5:33De 10:12
Deut. 5:33De 4:40; 12:28; Aro 10:5
  • Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
  • Werengani mu Baibulo la Dziko Latsopano
  • 1
  • 2
  • 3
  • 4
  • 5
  • 6
  • 7
  • 8
  • 9
  • 10
  • 11
  • 12
  • 13
  • 14
  • 15
  • 16
  • 17
  • 18
  • 19
  • 20
  • 21
  • 22
  • 23
  • 24
  • 25
  • 26
  • 27
  • 28
  • 29
  • 30
  • 31
  • 32
  • 33
Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
Deuteronomo 5:1-33

Deuteronomo

5 Ndiyeno Mose anaitana Aisiraeli onse nʼkuwauza kuti: “Inu Aisiraeli, mverani malangizo ndi zigamulo zimene ndikukuuzani lero, ndipo muziphunzire ndi kuzitsatira mosamala. 2 Yehova Mulungu wathu anachita nafe pangano ku Horebe.+ 3 Yehova sanachite pangano limeneli ndi makolo athu, koma ndi ife, tonse amene tili pano lero. 4 Yehova analankhula nanu pamasomʼpamaso mʼphiri, kuchokera mʼmoto.+ 5 Ine ndinaima pakati pa Yehova ndi inu pa nthawi imeneyo,+ kuti ndikuuzeni mawu a Yehova. Inuyo simunakwere mʼphirimo chifukwa munkaopa moto.+ Ndiyeno Mulungu anati:

6 ‘Ine ndine Yehova Mulungu wanu, amene ndinakutulutsani mʼdziko la Iguputo, mʼnyumba yaukapolo.+ 7 Musakhale ndi milungu ina iliyonse kupatulapo ine.*+

8 Musadzipangire fano kapena chifaniziro+ cha chinthu chilichonse chakumwamba, kapena chapadziko lapansi, kapenanso chamʼmadzi apadziko lapansi. 9 Musaziweramire kapena kuzitumikira,+ chifukwa ine Yehova Mulungu wanu, ndine Mulungu amene ndimafuna kuti anthu azidzipereka kwa ine ndekha,+ amene ndimalanga ana, zidzukulu ndi ana a zidzukuluzo chifukwa cha zolakwa za abambo a anthu odana ndi ine.+ 10 Koma ndimasonyeza chikondi chokhulupirika* kwa anthu mibadwo masauzande amene amandikonda komanso kusunga malamulo anga.

11 Musagwiritse ntchito dzina la Yehova Mulungu wanu molakwika,+ chifukwa Yehova sadzalekerera aliyense wogwiritsa ntchito dzina lake molakwika osamulanga.+

12 Muzisunga tsiku la Sabata ndipo muziliona kuti ndi lopatulika, mogwirizana ndi zimene Yehova Mulungu wanu anakulamulani.+ 13 Muzigwira ntchito zanu zonse masiku 6,+ 14 koma tsiku la 7 ndi sabata la Yehova Mulungu wanu.+ Musamagwire ntchito iliyonse,+ inuyo kapena mwana wanu wamwamuna, mwana wanu wamkazi, kapolo wanu wamwamuna, kapolo wanu wamkazi, ngʼombe yanu yamphongo, bulu wanu, chiweto chanu chilichonse, kapena mlendo amene akukhala mumzinda wanu,+ kuti nayenso kapolo wanu wamwamuna ndi kapolo wanu wamkazi, azipuma mofanana ndi inu.+ 15 Muzikumbukira kuti munali akapolo mʼdziko la Iguputo ndipo Yehova Mulungu wanu anakutulutsani kumeneko ndi dzanja lamphamvu komanso mkono wotambasula.+ Nʼchifukwa chake Yehova Mulungu wanu anakulamulani kuti muzisunga tsiku la Sabata.

16 Muzilemekeza bambo anu ndi mayi anu+ mogwirizana ndi zimene Yehova Mulungu wanu anakulamulani, kuti mukhale ndi moyo nthawi yaitali komanso kuti zinthu zikuyendereni bwino mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani.+

17 Musaphe munthu.*+

18 Musachite chigololo.+

19 Musabe.+

20 Musapereke umboni wonamizira mnzanu.+

21 Musalakelake mkazi wa mnzanu.+ Musalakelake mwadyera nyumba ya mnzanu, munda wake, kapolo wake wamwamuna, kapolo wake wamkazi, ngʼombe yake yamphongo, bulu wake, kapena chinthu chilichonse cha mnzanu.’+

22 Yehova anapereka malamulo* amenewa ku mpingo wanu wonse, mʼphiri. Analankhula mokweza kuchokera mʼmoto ndi mumtambo wakuda+ ndipo pa malamulowo sanawonjezerepo kalikonse. Kenako anawalemba pamiyala iwiri yosema nʼkundipatsa.+

23 Ndiyeno mutangomva mawu amenewo kuchokera pamalo amdima, phiri likuyaka moto,+ atsogoleri onse a mafuko anu ndi akulu onse anabwera kwa ine. 24 Ndiyeno munati, ‘Yehova Mulungu wathu watisonyeza ulemerero wake ndi ukulu wake, ndipo tamva mawu ake kuchokera mʼmoto.+ Lero taona kuti Mulungu angalankhule ndi munthu, munthuyo nʼkukhalabe ndi moyo.+ 25 Koma ife sitikufuna kufa, chifukwa moto waukuluwu ukhoza kutipsereza. Tikapitiriza kumvetsera mawu a Yehova Mulungu wathu ndithu tifa. 26 Kodi pali munthu aliyense amene anamvapo mawu a Mulungu wamoyo, akulankhula kuchokera mʼmoto ngati mmene ife tachitiramu nʼkukhalabe ndi moyo? 27 Iweyo upite pafupi ukamvetsere zonse zimene Yehova Mulungu wathu akanene. Ndiyeno iweyo udzatiuze zonse zimene Yehova Mulungu wathu wakuuza, ndipo ife tidzamvera nʼkuchita zomwezo.’+

28 Choncho Yehova anamva zonse zimene munandiuza, ndipo Yehova anandiuza kuti, ‘Ndamva mawu amene anthu awa akuuza. Zonse zimene anena ndi zabwino.+ 29 Zikanakhala bwino kwambiri akanakhala ndi mtima wondiopa+ ndi kusunga malamulo anga+ nthawi zonse. Akanachita zimenezi zinthu zikanawayendera bwino, iwowo ndi ana awo mpaka kalekale!+ 30 Pita ukawauze kuti: “Bwererani kumatenti anu.” 31 Koma iwe ukhale pompano, ndipo ndikuuza malamulo onse, malangizo ndi zigamulo zimene ukuyenera kuwaphunzitsa kuti azikazitsatira mʼdziko limene ndikuwapatsa kuti likhale lawo.’ 32 Ndipo anthu inu muonetsetse kuti mukuchita zimene Yehova Mulungu wanu wakulamulani.+ Musatembenukire kudzanja lamanja kapena lamanzere.+ 33 Muziyenda mʼnjira imene Yehova Mulungu wanu wakulamulani,+ kuti mukhale ndi moyo, kuti zinthu zikuyendereni bwino komanso kuti mukhale ndi moyo wautali mʼdziko limene mudzalitenge kuti likhale lanu.”+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena