Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Deuteronomo 2
  • Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

Zimene Zili Mʼbuku la Deuteronomo

      • Anayenda mʼchipululu kwa zaka 38 (1-23)

      • Anagonjetsa Mfumu Sihoni ya ku Hesiboni (24-37)

Deuteronomo 2:1

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Nu 14:25

Deuteronomo 2:4

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Nu 20:14; De 23:7
  • +Ge 27:39, 40; 36:8, 9
  • +Eks 15:15; 23:27

Deuteronomo 2:5

Mawu a M'munsi

  • *

    Kapena kuti, “Musawavutitse.”

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +De 32:8; Yos 24:4; Mac 17:26

Deuteronomo 2:6

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Nu 20:18, 19

Deuteronomo 2:7

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +De 29:5; Ne 9:21; Sl 23:1; 34:9, 10

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Nsanja ya Olonda (Yophunzira),

    1/2022, ptsa. 5-6

Deuteronomo 2:8

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Nu 20:20, 21
  • +2Mb 8:17
  • +Nu 21:13; Owe 11:17, 18; 2Mb 20:10

Deuteronomo 2:9

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Ge 19:36, 37

Deuteronomo 2:10

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Ge 14:5

Deuteronomo 2:11

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +De 3:11; 1Mb 20:6
  • +Nu 13:22, 33

Deuteronomo 2:12

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Ge 14:6; 36:20
  • +Ge 27:39, 40

Deuteronomo 2:13

Mawu a M'munsi

  • *

    Kapena kuti, “khwawa la Zeredi.”

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Nu 21:12

Deuteronomo 2:14

Mawu a M'munsi

  • *

    Kapena kuti, “khwawa la Zeredi.”

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Nu 14:33; 32:11; De 1:35; Sl 95:11; Ahe 3:18; Yuda 5

Deuteronomo 2:15

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +1Ak 10:1, 5

Deuteronomo 2:16

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Nu 26:63, 64

Deuteronomo 2:19

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Ge 19:36, 38; De 2:9; Owe 11:15; 2Mb 20:10; Mac 17:26

Deuteronomo 2:20

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Ge 15:18-20; De 3:11

Deuteronomo 2:21

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Nu 13:33; De 9:1, 2

Deuteronomo 2:22

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Ge 36:8
  • +Ge 14:6; De 2:12

Deuteronomo 2:23

Mawu a M'munsi

  • *

    Kutanthauza Kerete.

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Ge 10:19
  • +Ge 10:13, 14

Deuteronomo 2:24

Mawu a M'munsi

  • *

    Kapena kuti, “khwawa la Arinoni.”

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Nu 21:13
  • +Nu 21:23

Deuteronomo 2:25

Mawu a M'munsi

  • *

    Kapena kuti, “adzamva ululu ngati umene munthu amamva pobereka.”

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Eks 15:14; 23:27; De 11:25; Yos 2:9, 10

Deuteronomo 2:26

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Yos 13:15, 18; 21:8, 37
  • +De 20:10

Deuteronomo 2:27

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Nu 21:21, 22

Deuteronomo 2:30

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Aro 9:18
  • +Nu 21:25

Deuteronomo 2:31

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Nu 32:33; Sl 135:10-12

Deuteronomo 2:32

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Nu 21:23, 24; Owe 11:20

Deuteronomo 2:34

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +De 20:16, 17

Deuteronomo 2:36

Mawu a M'munsi

  • *

    Kapena kuti, “khwawa la Arinoni.”

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +De 3:12; 4:47, 48; Yos 13:8, 9
  • +Sl 44:3

Deuteronomo 2:37

Mawu a M'munsi

  • *

    Kapena kuti, “khwawa la Yaboki.”

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +De 3:16; Owe 11:15
  • +Nu 21:23, 24

Mabaibulo Ena

Dinani pa nambala ya vesi kuti muone mavesi a m'Baibulo lina ofanana ndi vesilo.

Malemba Ena

Deut. 2:1Nu 14:25
Deut. 2:4Nu 20:14; De 23:7
Deut. 2:4Ge 27:39, 40; 36:8, 9
Deut. 2:4Eks 15:15; 23:27
Deut. 2:5De 32:8; Yos 24:4; Mac 17:26
Deut. 2:6Nu 20:18, 19
Deut. 2:7De 29:5; Ne 9:21; Sl 23:1; 34:9, 10
Deut. 2:8Nu 20:20, 21
Deut. 2:82Mb 8:17
Deut. 2:8Nu 21:13; Owe 11:17, 18; 2Mb 20:10
Deut. 2:9Ge 19:36, 37
Deut. 2:10Ge 14:5
Deut. 2:11De 3:11; 1Mb 20:6
Deut. 2:11Nu 13:22, 33
Deut. 2:12Ge 14:6; 36:20
Deut. 2:12Ge 27:39, 40
Deut. 2:13Nu 21:12
Deut. 2:14Nu 14:33; 32:11; De 1:35; Sl 95:11; Ahe 3:18; Yuda 5
Deut. 2:151Ak 10:1, 5
Deut. 2:16Nu 26:63, 64
Deut. 2:19Ge 19:36, 38; De 2:9; Owe 11:15; 2Mb 20:10; Mac 17:26
Deut. 2:20Ge 15:18-20; De 3:11
Deut. 2:21Nu 13:33; De 9:1, 2
Deut. 2:22Ge 36:8
Deut. 2:22Ge 14:6; De 2:12
Deut. 2:23Ge 10:19
Deut. 2:23Ge 10:13, 14
Deut. 2:24Nu 21:13
Deut. 2:24Nu 21:23
Deut. 2:25Eks 15:14; 23:27; De 11:25; Yos 2:9, 10
Deut. 2:26Yos 13:15, 18; 21:8, 37
Deut. 2:26De 20:10
Deut. 2:27Nu 21:21, 22
Deut. 2:30Aro 9:18
Deut. 2:30Nu 21:25
Deut. 2:31Nu 32:33; Sl 135:10-12
Deut. 2:32Nu 21:23, 24; Owe 11:20
Deut. 2:34De 20:16, 17
Deut. 2:36De 3:12; 4:47, 48; Yos 13:8, 9
Deut. 2:36Sl 44:3
Deut. 2:37De 3:16; Owe 11:15
Deut. 2:37Nu 21:23, 24
  • Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
  • Werengani mu Baibulo la Dziko Latsopano
  • 1
  • 2
  • 3
  • 4
  • 5
  • 6
  • 7
  • 8
  • 9
  • 10
  • 11
  • 12
  • 13
  • 14
  • 15
  • 16
  • 17
  • 18
  • 19
  • 20
  • 21
  • 22
  • 23
  • 24
  • 25
  • 26
  • 27
  • 28
  • 29
  • 30
  • 31
  • 32
  • 33
  • 34
  • 35
  • 36
  • 37
Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
Deuteronomo 2:1-37

Deuteronomo

2 “Ndiyeno tinatembenuka nʼkulowera kuchipululu kudzera njira ya ku Nyanja Yofiira, mogwirizana ndi zimene Yehova anandiuza.+ Ndipo tinayenda masiku ambiri mʼdera lapafupi ndi phiri la Seiri. 2 Kenako Yehova anandiuza kuti, 3 ‘Mwayenda kwa nthawi yaitali mʼdera lapafupi ndi phirili. Tsopano mulowere kumpoto. 4 Auze anthuwo kuti: “Mudutsa mʼmalire a dziko la abale anu, mbadwa za Esau,+ amene akukhala ku Seiri.+ Iwo adzachita nanu mantha,+ choncho muyenera kukhala osamala kwambiri. 5 Musalimbane nawo,* chifukwa sindikupatsani mbali iliyonse ya dziko lawo, ngakhale kachigawo kokwana phazi limodzi lokha, chifukwa ndinapereka phiri la Seiri kwa Esau kuti likhale malo ake.+ 6 Mudzawapatse ndalama pa chakudya chimene mudzadye, ndipo mudzapereke ndalama pa madzi amene mudzamwe.+ 7 Chifukwa Yehova Mulungu wanu wakudalitsani pa chilichonse chimene mukuchita. Iye akudziwa bwino kuti mukuyenda mʼchipululu chachikuluchi. Yehova Mulungu wanu wakhala nanu zaka 40 zimenezi, ndipo simunasowe kanthu.”’+ 8 Choncho tinadutsa pafupi ndi abale athu, mbadwa za Esau,+ amene akukhala ku Seiri, ndipo sitinayende njira ya Araba, Elati ndi Ezioni-geberi.+

Kenako tinatembenuka nʼkudutsa njira ya mʼchipululu cha Mowabu.+ 9 Ndiyeno Yehova anandiuza kuti, ‘Usalimbane ndi Amowabu kapena kuchita nawo nkhondo, chifukwa sindidzakupatsa mbali iliyonse ya dziko lawo kuti likhale lako. Ndinapereka Ari kwa mbadwa za Loti+ kuti akhale malo awo. 10 (Kale mʼdzikoli munkakhala Aemi,+ anthu amphamvu kwambiri ndiponso ochuluka. Iwo anali ataliatali ngati Aanaki. 11 Arefai+ nawonso ankaoneka ngati Aanaki,+ ndipo Amowabu ankawatchula kuti Aemi. 12 Poyamba, Ahori+ ankakhala ku Seiri, koma mbadwa za Esau zinawalanda dzikolo nʼkuwapha ndipo iwo anayamba kukhala mʼdzikolo,+ mofanana ndi zimene Aisiraeli adzachite ndi dziko limene ndi cholowa chawo, limene Yehova adzawapatsadi.) 13 Tsopano nyamukani muwoloke chigwa cha Zeredi.’* Choncho tinawolokadi chigwa cha Zeredi.+ 14 Panadutsa zaka 38 kuti tiyende kuchokera ku Kadesi-barinea nʼkuwoloka chigwa cha Zeredi,* mpaka mʼbadwo wonse wa amuna opita kunkhondo utatha pakati pathu, mogwirizana ndi zimene Yehova analumbira kwa iwo.+ 15 Pogwiritsa ntchito dzanja lake, Yehova anawachotsa pakati panu mpaka onse anatha.+

16 Amuna onse opita kunkhondo pakati pa anthuwo atatha kufa,+ 17 Yehova analankhulanso ndi ine kuti, 18 ‘Lero mudutsa malire a dziko la Mowabu, kapena kuti Ari. 19 Mukafika pafupi ndi Aamoni, musawavutitse kapena kulimbana nawo, chifukwa sindidzakupatsani mbali iliyonse ya dziko la Aamoni kuti likhale lanu. Dziko limeneli ndinalipereka kwa mbadwa za Loti kuti likhale lawo.+ 20 Dziko limenelinso linkadziwika kuti ndi la Arefai.+ (Kale mʼdzikoli munkakhala Arefai ndipo Aamoni ankawatchula kuti Azamuzumi. 21 Anthu amenewa anali amphamvu kwambiri komanso ochuluka ndipo anali ataliatali ngati Aanaki.+ Koma Yehova anawagonjetsa pamaso pa Aamoni, ndipo Aamoniwo anawathamangitsa moti anatenga dzikolo nʼkumakhalamo. 22 Mulungu anachitanso zimenezi kwa mbadwa za Esau zimene zikukhala ku Seiri.+ Iye anagonjetsa Ahori+ pamaso pawo kuti mbadwa za Esauzo zitenge dzikolo nʼkumakhalamo mpaka lero. 23 Koma Aavi ankakhala mʼmidzi mpaka kukafika ku Gaza.+ Iwo ankakhala mʼmidzi imeneyi mpaka pamene Akafitorimu+ ochokera ku Kafitori,* anawawononga nʼkuyamba kukhala mʼmidzi yawoyo.)

24 Nyamukani ndipo muwoloke chigwa cha Arinoni.*+ Taonani, ndapereka mʼmanja mwanu Sihoni+ yemwe ndi munthu wa Chiamori, mfumu ya Hesiboni. Choncho yambani kulanda dziko lake ndipo muchite naye nkhondo. 25 Lero ndichititsa kuti anthu onse okhala pansi pa thambo, amene amva za inu, achite nanu mantha kwambiri nʼkuyamba kukuopani. Iwo adzasokonezeka maganizo ndipo adzanjenjemera* chifukwa cha inu.’+

26 Kenako ndinatumiza amithenga kuchokera mʼchipululu cha Kademoti+ kupita kwa Mfumu Sihoni ya ku Hesiboni, kuti akanene uthenga wamtendere kuti,+ 27 ‘Ndilole ndidutse mʼdziko lako. Ndidzangodutsa mumsewu ndipo sindidzakhotera kudzanja lamanja kapena lamanzere.+ 28 Ndidzadya chakudya komanso kumwa madzi amene udzandigulitse. Ungondilola kuti ndidutse mʼdziko lako 29 mpaka kukawoloka Yorodano nʼkulowa mʼdziko limene Yehova Mulungu wathu anatipatsa. Izi nʼzimene mbadwa za Esau zimene zikukhala ku Seiri komanso Amowabu amene akukhala ku Ari anandichitira.’ 30 Koma Mfumu Sihoni ya ku Hesiboni sinatilole kuti tidutse mʼdziko lake, chifukwa Yehova Mulungu wanu anamulola kuti akhale wokanika+ komanso kuti aumitse mtima wake, nʼcholinga choti amupereke mʼmanja mwanu monga mmene zilili lero.+

31 Kenako Yehova anandiuza kuti, ‘Taona, ndayamba kale kupereka Sihoni ndi dziko lake kwa iwe. Yamba kulanda dziko lake.’+ 32 Sihoni atatuluka pamodzi ndi anthu ake onse kudzamenya nafe nkhondo ku Yahazi,+ 33 Yehova Mulungu wathu anamupereka kwa ife ndipo tinamugonjetsa limodzi ndi ana ake komanso anthu ake onse. 34 Pa nthawi imeneyo, tinalanda mizinda yake yonse ndi kuwononga mzinda wina uliwonse. Tinapha amuna, akazi ndi ana ndipo sitinasiye munthu aliyense ndi moyo.+ 35 Ziweto zokha nʼzimene tinatenga pamodzi ndi zinthu zimene tinatenga mʼmizinda imene tinalanda. 36 Kuchokera ku Aroweli,+ mzinda umene uli mʼmbali mwa chigwa cha Arinoni,* (kuphatikizapo mzinda umene uli mʼchigwacho), mpaka kukafika ku Giliyadi, panalibe mzinda umene sitinathe kuugonjetsa. Yehova Mulungu wathu anawapereka onsewo kwa ife.+ 37 Koma simunayandikire dziko la Aamoni,+ dera lonse lamʼmbali mwa chigwa cha Yaboki,*+ kapena mizinda yamʼdera lamapiri, kapenanso malo alionse amene Yehova Mulungu wathu anatiletsa.”

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena