Genesis 30:2 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 2 Pamenepo Yakobo anamupsera mtima kwambiri Rakele n’kumuyankha kuti:+ “Kodi ine ndine Mulungu amene akukulepheretsa kuberekayo?”+ Genesis 41:52 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 52 Wachiwiriyo anamutcha Efuraimu,*+ chifukwa anati, “Mulungu wandipatsa ana m’dziko la masautso anga.”+ Levitiko 26:9 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 9 “‘Pamenepo ndidzakucheukirani,+ kukuchititsani kubereka ana ambiri ndi kukuchulukitsani.+ Ndipo ndidzasunga pangano langa ndi inu.+ Deuteronomo 28:4 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 4 “Chidzadalitsika chipatso cha mimba yako,+ chipatso cha m’dziko lanu, chipatso cha ziweto zako,+ ana a ng’ombe zako ndi ana a nkhosa zako.+ Yoswa 24:3 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 3 “‘Patapita nthawi, ndinatenga Abulahamu+ tate wanu, kuchokera kutsidya lina la Mtsinje,+ ndipo ndinamuyendetsa m’dziko lonse la Kanani, ndi kuchulukitsa mbewu yake.+ Chotero ndinam’dalitsa ndipo anabereka Isaki,+ Yoswa 24:4 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 4 Isaki anabereka Yakobo ndi Esau.+ Pambuyo pake Esau ndinam’patsa phiri la Seiri kuti likhale lake.+ Kenako, Yakobo ndi ana ake anapita ku Iguputo.+ Salimo 128:3 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 3 Mkazi wako adzakhala ngati mtengo wa mpesa wobala zipatso+Mkati mwa nyumba yako.Ana ako adzakhala ngati mphukira za mitengo ya maolivi+ kuzungulira tebulo lako. Yesaya 8:18 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 18 Taonani, ine ndi ana amene Yehova wandipatsa+ tili ngati zizindikiro+ ndiponso ngati zozizwitsa mu Isiraeli, zochokera kwa Yehova wa makamu amene amakhala m’phiri la Ziyoni.+
2 Pamenepo Yakobo anamupsera mtima kwambiri Rakele n’kumuyankha kuti:+ “Kodi ine ndine Mulungu amene akukulepheretsa kuberekayo?”+
52 Wachiwiriyo anamutcha Efuraimu,*+ chifukwa anati, “Mulungu wandipatsa ana m’dziko la masautso anga.”+
9 “‘Pamenepo ndidzakucheukirani,+ kukuchititsani kubereka ana ambiri ndi kukuchulukitsani.+ Ndipo ndidzasunga pangano langa ndi inu.+
4 “Chidzadalitsika chipatso cha mimba yako,+ chipatso cha m’dziko lanu, chipatso cha ziweto zako,+ ana a ng’ombe zako ndi ana a nkhosa zako.+
3 “‘Patapita nthawi, ndinatenga Abulahamu+ tate wanu, kuchokera kutsidya lina la Mtsinje,+ ndipo ndinamuyendetsa m’dziko lonse la Kanani, ndi kuchulukitsa mbewu yake.+ Chotero ndinam’dalitsa ndipo anabereka Isaki,+
4 Isaki anabereka Yakobo ndi Esau.+ Pambuyo pake Esau ndinam’patsa phiri la Seiri kuti likhale lake.+ Kenako, Yakobo ndi ana ake anapita ku Iguputo.+
3 Mkazi wako adzakhala ngati mtengo wa mpesa wobala zipatso+Mkati mwa nyumba yako.Ana ako adzakhala ngati mphukira za mitengo ya maolivi+ kuzungulira tebulo lako.
18 Taonani, ine ndi ana amene Yehova wandipatsa+ tili ngati zizindikiro+ ndiponso ngati zozizwitsa mu Isiraeli, zochokera kwa Yehova wa makamu amene amakhala m’phiri la Ziyoni.+