Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Levitiko 6:2
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 2 “Munthu akachimwa mwa kuchita mosakhulupirika kwa Yehova+ chifukwa wanyenga+ mnzake pa chinthu chimene chili m’manja mwake, kapena chimene mnzake wam’sungitsa,+ kapena wafwamba mnzake, kapena wam’bera mwachinyengo,+

  • Yesaya 1:23
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 23 Akalonga ako ndi aliuma ndipo ndi anzawo a mbala.+ Aliyense wa iwo amakonda ziphuphu+ ndipo amafunafuna mphatso.+ Mwana wamasiye samuweruza mwachilungamo ndipo ngakhale mlandu wa mkazi wamasiye safuna kuuweruza.+

  • Yeremiya 5:26
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 26 “‘Zili choncho, chifukwa pakati pa anthu anga papezeka anthu oipa.+ Iwo amawabisalira ndi kuwayang’anitsitsa ngati mmene wosaka mbalame amachitira.+ Awatchera msampha wowononga pakuti iwo amagwira anthu.

  • Yeremiya 7:9
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 9 Kodi mungamabe,+ kupha,+ kuchita chigololo,+ kulumbira monama,+ kufukiza nsembe zautsi kwa Baala+ ndi kutsatira milungu ina imene simunali kuidziwa,+

  • Yeremiya 21:12
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 12 Inu a m’nyumba ya Davide,+ Yehova wanena kuti: “M’mawa uliwonse+ muziweruza mwachilungamo,+ ndipo muzilanditsa munthu kwa anthu achinyengo amene akufuna kumulanda katundu.+ Muzitero kuti mkwiyo wanga usayake ngati moto+ ndi kukutenthani popanda wouzimitsa chifukwa cha kuipa kwa zochita zanu.”’+

  • Mika 2:2
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 2 Iwo alakalaka minda ya anthu ena ndipo ailanda.+ Alakalakanso nyumba za anthu ena n’kuzitenga kukhala zawo.+ Atenga mwachinyengo cholowa cha munthu ndi cha banja lake.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena