Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Deuteronomo 12:31
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 31 Usapembedze Yehova Mulungu wako m’njira imeneyi,+ pakuti iwo amachitira milungu yawo zonse zimene zili zonyansa kwa Yehova, zimene iye amadana nazo. Pakuti iwo nthawi zonse amatentha ana awo aamuna ndi aakazi pamoto monga nsembe kwa milungu yawo.+

  • 1 Mafumu 11:7
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 7 Panali pa nthawi imeneyi pamene Solomo anamangira Kemosi+ malo okwezeka,+ chinthu chonyansa+ cha Mowabu, paphiri+ lomwe linali patsogolo+ pa Yerusalemu. Anamangiranso Moleki malo okwezeka, yemwe ndi chinthu chonyansa cha ana a Amoni.

  • 2 Mafumu 17:17
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 17 Iwo anapitiriza kuwotcha* pamoto+ ana awo aamuna ndi aakazi, kulosera+ ndi kuwombeza.*+ Anapitirizanso+ kuchita zoipa* pamaso pa Yehova ndi cholinga chomukwiyitsa.+

  • 2 Mbiri 28:3
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 3 Ahazi anafukiza nsembe yautsi+ m’chigwa cha mwana wa Hinomu.+ Iye anawotcha ana ake+ pamoto mofanana ndi zonyansa+ za anthu a mitundu ina amene Yehova anawapitikitsa pamaso pa ana a Isiraeli.+

  • Salimo 106:37
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 37 Anali kupereka nsembe ana awo aamuna+

      Ndi ana awo aakazi kwa ziwanda.+

  • Yeremiya 7:31
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 31 Iwo amanga malo okwezeka ku Tofeti,+ m’chigwa cha mwana wa Hinomu,+ kuti azitentha ana awo aamuna ndi ana awo aakazi pamoto,+ chinthu chimene sindinawalamule kuchita ndiponso chimene sindinachiganizirepo mumtima mwanga.’+

  • Ezekieli 16:20
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 20 “‘Unali kutenga ana ako aamuna ndi aakazi amene unandiberekera+ n’kumawapereka nsembe kwa mafano.+ Kodi zochita zako zauhulezo sizinakukwanire?

  • 1 Akorinto 10:20
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 20 Ayi, koma ndikunena kuti zinthu zimene mitundu ina imapereka nsembe imazipereka kwa ziwanda,+ osati kwa Mulungu, ndipo sindikufuna kuti mukhale ogawana ndi ziwanda.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena