-
2 Mafumu 23:5Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
5 Mfumuyo inachotsa ntchito ansembe a milungu yachilendo, amene mafumu a Yuda anawaika kuti azifukiza nsembe yautsi pamalo okwezeka m’mizinda ya Yuda ndi malo ozungulira Yerusalemu. Inachotsanso ntchito ansembe ofukiza nsembe yautsi kwa Baala,+ kwa dzuwa, kwa mwezi, kwa magulu a nyenyezi, ndi kwa khamu lonse la zinthu zakuthambo.+
-
-
Yobu 31:26Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
26 Ngati ndinkaona kuwala kukamanyezimira,
Kapena mwezi wamtengo wapatali ukuyenda,+
-
Yeremiya 8:2Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
2 Mafupawo adzawamwaza poyera ndipo dzuwa, mwezi, ndi makamu onse akumwamba zidzawala pa iwo. Zinthu zimenezi ndi zimene iwo anali kuzikonda, kuzitumikira, kuzitsatira,+ kuzipembedza, ndi kuziweramira.+ Mafupawo sadzasonkhanitsidwa pamodzi kapena kuikidwa m’manda. Iwo adzakhala ngati manyowa panthaka.”+
-
-
Yeremiya 44:17Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
17 Ife tichita zonse zimene tanena.+ Tipereka nsembe zautsi ndi kuthira nsembe zachakumwa+ kwa ‘mfumukazi yakumwamba.’+ Tichita zimenezi monga mmene ife,+ makolo athu,+ mafumu athu+ ndi akalonga athu anachitira m’mizinda ya Yuda ndi m’misewu ya Yerusalemu pamene tinali kudya mkate ndi kukhuta ndipo zinthu zinali kutiyendera bwino, moti sitinaone tsoka lililonse.+
-
-
-