Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Oweruza 14:3
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 3 Koma bambo ndi mayi akewo anam’funsa kuti: “Kodi wasowa mkazi pakati pa ana aakazi a abale ako ndi anthu onse a mtundu wathu,+ kuti upite kukatenga mkazi kwa Afilisiti osadulidwa?”+ Koma Samisoni anauza atate akewo kuti: “Ingonditengerani mkazi ameneyu, chifukwa ndi amene ali woyenera kwa ine?”

  • 1 Samueli 17:26
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 26 Ndiyeno Davide anayamba kufunsa amuna amene anali ataimirira pafupi naye kuti: “Kodi munthu amene angakaphe Mfilisiti+ ameneyu ndi kuchotsa chitonzo pa Isiraeli+ amuchitira chiyani? Kodi Mfilisiti wosadulidwa+ ameneyu ndani kuti azinyoza+ asilikali a Mulungu wamoyo?”+

  • 1 Samueli 17:36
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 36 Mtumiki wanu anapha zonse ziwiri, mkangowo ndi chimbalangondocho. Mfilisiti wosadulidwayu+ akhalanso ngati chimodzi mwa zilombo zimenezi, chifukwa watonza+ asilikali+ a Mulungu wamoyo.”+

  • 1 Samueli 21:11
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 11 Atafika kumeneko, atumiki a Akisi anayamba kunena kuti: “Kodi ameneyu si Davide+ mfumu ya dziko? Suja ankamuimbira nyimbo molandizana mawu, akuvina+ n’kumati,

      ‘Sauli wakantha adani ake masauzande,

      Ndipo Davide wakantha masauzande makumimakumi’?”+

  • 2 Samueli 1:20
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 20 Anthu inu musanene zimenezi mumzinda wa Gati.+

      Musalengeze zimenezi m’misewu ya Asikeloni,+

      Kuopera kuti ana aakazi a Afilisiti angasangalale,+

      Kuopera kuti ana aakazi a anthu osadulidwa angakondwere.

  • 2 Samueli 3:14
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 14 Davide anatumizanso mithenga kwa Isi-boseti+ mwana wa Sauli ndi uthenga wonena kuti: “Ndipatse mkazi wanga Mikala, amene ndinalonjeza kumukwatira mwa kupereka makungu 100 akunsonga+ a Afilisiti.”

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena